Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (22) Surah: Soerat Ibrahim (Abraham)
وَقَالَ ٱلشَّيۡطَٰنُ لَمَّا قُضِيَ ٱلۡأَمۡرُ إِنَّ ٱللَّهَ وَعَدَكُمۡ وَعۡدَ ٱلۡحَقِّ وَوَعَدتُّكُمۡ فَأَخۡلَفۡتُكُمۡۖ وَمَا كَانَ لِيَ عَلَيۡكُم مِّن سُلۡطَٰنٍ إِلَّآ أَن دَعَوۡتُكُمۡ فَٱسۡتَجَبۡتُمۡ لِيۖ فَلَا تَلُومُونِي وَلُومُوٓاْ أَنفُسَكُمۖ مَّآ أَنَا۠ بِمُصۡرِخِكُمۡ وَمَآ أَنتُم بِمُصۡرِخِيَّ إِنِّي كَفَرۡتُ بِمَآ أَشۡرَكۡتُمُونِ مِن قَبۡلُۗ إِنَّ ٱلظَّٰلِمِينَ لَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndipo satana adzanena chiweruzo chikadzalamulidwa (oipa kulowa ku Moto, abwino kulowa ku Munda wamtendere): “Ndithu Allah adakulonjezani lonjezo loona (ndipo wakwaniritsa). Nane ndidakulonjezani, koma sindidakukwaniritsireni. Ndidalibe mphamvu pa inu (yokukakamizirani kunditsata) koma ndimangokuitanani basi, ndipo munkandiyankha. Choncho musandidzudzule, koma dzidzudzuleni nokha. Sindingathe kukuthangatani ndiponso inu simungathe kundithangata. Ndithu ine ndidakukana kundiphatikiza kwanu ndi Allah kale. Ndithu ochita zoipa adzapeza chilango chowawa.”[242]
[242] Omasulira Qur’an adati: Chiweruzo chikadzaweruzidwa, anthu abwino nkukakhazikika ku Munda wa mtendere pomwe anthu oipa nkukalowa ku Moto, anthu a ku Moto adzayamba kumadzudzula satana ndi kumnyoza. Ndipo satana adzaimilira pakati pawo pagome la Moto m’katikati mwa Jahannam nadzanena kwa anthu onse a ku Moto kuti: “Musandidzudzule, koma dzudzulani mitima yanu. Mitima yanu ndiyomwe idakuonongani. Ine ndinkangokuitanani chabe, sindidakukakamizeni.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (22) Surah: Soerat Ibrahim (Abraham)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit