Check out the new design

Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: De bij   Vers:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ أَشۡرَكُواْ لَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَا عَبَدۡنَا مِن دُونِهِۦ مِن شَيۡءٖ نَّحۡنُ وَلَآ ءَابَآؤُنَا وَلَا حَرَّمۡنَا مِن دُونِهِۦ مِن شَيۡءٖۚ كَذَٰلِكَ فَعَلَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡۚ فَهَلۡ عَلَى ٱلرُّسُلِ إِلَّا ٱلۡبَلَٰغُ ٱلۡمُبِينُ
Ndipo aja amapembedza mafano akuti: “Allah akadafuna, sitikadapembedza chilichonse kusiya Iye, ife ngakhale makolo athu; ndiponso palibe chomwe tikadachiyesa choletsedwa popanda lamulo Lake.” Momwemo ndimo adachitiranso aja omwe adalipo patsogolo pawo. Kodi atumiki ali ndi udindo winanso, osati kufikitsa uthenga woonekera (womveka?)
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَقَدۡ بَعَثۡنَا فِي كُلِّ أُمَّةٖ رَّسُولًا أَنِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ وَٱجۡتَنِبُواْ ٱلطَّٰغُوتَۖ فَمِنۡهُم مَّنۡ هَدَى ٱللَّهُ وَمِنۡهُم مَّنۡ حَقَّتۡ عَلَيۡهِ ٱلضَّلَٰلَةُۚ فَسِيرُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَٱنظُرُواْ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُكَذِّبِينَ
Ndipo ndithu ku mtundu uliwonse tidatumiza mtumiki (amene amawauza kuti): “Pembedzani Allah, ndi kumpewa (Iblis) woipa.” Choncho alipo ena mwa iwo omwe Allah adawaongola, ndipo alipo ena mwa iwo omwe kusokera kudatsimikizika pa iwo. Choncho yendani pa dziko ndikuyang’ana (kuti) kodi adali bwanji mathero a otsutsa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِن تَحۡرِصۡ عَلَىٰ هُدَىٰهُمۡ فَإِنَّ ٱللَّهَ لَا يَهۡدِي مَن يُضِلُّۖ وَمَا لَهُم مِّن نَّٰصِرِينَ
Ngati uwumilira kwambiri kuti uwaongole, komatu Allah saongola yemwe akusokeretsa (ena), ndipo sadzapeza wowathangata.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَأَقۡسَمُواْ بِٱللَّهِ جَهۡدَ أَيۡمَٰنِهِمۡ لَا يَبۡعَثُ ٱللَّهُ مَن يَمُوتُۚ بَلَىٰ وَعۡدًا عَلَيۡهِ حَقّٗا وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo iwo adalumbilira m’dzina la Allah, kulumbilira kwawo kwamphamvu (kuti) Allah sadzaukitsa amene afa; nchotani (kuti asawaukitse?) Ili ndi lonjezo lokakamizika kwa Iye, (kuwaukitsa ndi kuwalipira); koma anthu ambiri sadziwa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِيُبَيِّنَ لَهُمُ ٱلَّذِي يَخۡتَلِفُونَ فِيهِ وَلِيَعۡلَمَ ٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ أَنَّهُمۡ كَانُواْ كَٰذِبِينَ
(Adzawaukitsa) kuti awafotokozere za zomwe adali kusiyana ndi kuti amene sadakhulupirire adziwe kuti ndithu iwo adali abodza.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّمَا قَوۡلُنَا لِشَيۡءٍ إِذَآ أَرَدۡنَٰهُ أَن نَّقُولَ لَهُۥ كُن فَيَكُونُ
Ndithu liwu Lathu pa chinthu chimene tikuchifuna kuti chichitike ndikuchiuza basi kuti: “Chitika,” ndipo chimachitikadi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّذِينَ هَاجَرُواْ فِي ٱللَّهِ مِنۢ بَعۡدِ مَا ظُلِمُواْ لَنُبَوِّئَنَّهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا حَسَنَةٗۖ وَلَأَجۡرُ ٱلۡأٓخِرَةِ أَكۡبَرُۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Ndipo omwe adasamuka chifukwa cha Allah (kusiya midzi yawo) pambuyo poponderezedwa (kumeneko,) ndithu tiwakhazika mwaubwino pa dziko lapansi; ndipo malipiro a tsiku la chimaliziro (omwe akuwayembekezera), ngakulu zedi, akadakhala akudziwa (awa oipa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
ٱلَّذِينَ صَبَرُواْ وَعَلَىٰ رَبِّهِمۡ يَتَوَكَّلُونَ
(Amene adzapeza zimenezi, ndi) omwe adapirira ndi kutsamira kwa Mbuye wawo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: De bij
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala - Index van vertaling

Vertaald door Khalid Ibrahim Bitala.

Sluit