Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (217) Surah: Soerat Albaqarah (De Koe)
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلشَّهۡرِ ٱلۡحَرَامِ قِتَالٖ فِيهِۖ قُلۡ قِتَالٞ فِيهِ كَبِيرٞۚ وَصَدٌّ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ وَكُفۡرُۢ بِهِۦ وَٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ وَإِخۡرَاجُ أَهۡلِهِۦ مِنۡهُ أَكۡبَرُ عِندَ ٱللَّهِۚ وَٱلۡفِتۡنَةُ أَكۡبَرُ مِنَ ٱلۡقَتۡلِۗ وَلَا يَزَالُونَ يُقَٰتِلُونَكُمۡ حَتَّىٰ يَرُدُّوكُمۡ عَن دِينِكُمۡ إِنِ ٱسۡتَطَٰعُواْۚ وَمَن يَرۡتَدِدۡ مِنكُمۡ عَن دِينِهِۦ فَيَمُتۡ وَهُوَ كَافِرٞ فَأُوْلَٰٓئِكَ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Akukufunsa za (lamulo la) kumenya nkhondo m’miyezi yopatulika. nena: “Kumenya nkhondo m’miyeziyo ndi tchimo lalikulu. Komatu kuwatsekereza anthu ku njira ya Allah, ndi kumkana Allah, (ndi kuletsa anthu) ku Msikiti Wopatulikawo, ndi kutulutsa anthu m’menemo nditchimo loposa kwa Allah. Ndipo kutsekereza anthu kuchipembedzo chawo nzoipa kwabasi kuposa kupha. Ndipo sasiya kumenyana nanu kufikira akuchotseni m’chipembedzo chanu ngati angathe. Ndipo mwa inu amene atuluke m’chipembedzo chake, kenako namwalira uku ali osakhulipirira, iwo ndi omwe ntchito zawo zaonongeka pa dziko lapansi mpaka tsiku lachimaliziro. Ndipo iwo ndi anthu a ku Moto. M’menemo adzakhalamo nthawi yaitali.[30]
[30] Otsatira Mneneri (maswahaba) anakumana ndi osakhulupilira padeti ya 30, m’mwezi wa 6 pakalendala ya Chisilamu. Ena amaganiza kuti detilo la pa 30 lidali la m’mwezi wa Rajabu omwe ngoletsedwa kuchitamo nkhondo. Tero Aquraish adamnamizira Muhammad (s.a.w) kuti waswa ulemelero wa miyezi yopatulika. Ndipo adabwera kukamfunsa kuti: “Kodi ndimmene ukuchitira?” Umo ndi momwe Allah adawayankhira.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (217) Surah: Soerat Albaqarah (De Koe)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit