Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (31) Surah: Soerat An-nisa (de vrouwen)
إِن تَجۡتَنِبُواْ كَبَآئِرَ مَا تُنۡهَوۡنَ عَنۡهُ نُكَفِّرۡ عَنكُمۡ سَيِّـَٔاتِكُمۡ وَنُدۡخِلۡكُم مُّدۡخَلٗا كَرِيمٗا
Ngati mudzitalikitsa kumachimo akuluakulu omwe mukuletsedwa, ndiye kuti tikufafanizirani zolakwa zanu (zing’onozing’ono) ndipo tidzakulowetsani malo aulemu.[119]
[119] Apa akuti ngati tipewa machimo akuluakulu, Allah adzatikhululukira timachimo ting’onoting’ono. Munthu nkovuta kuupewa uchimo ung’onoung’ono. Uchimotu suli wofanana. Pali wina waukulu. Palinso wina wokulitsitsa. Ndipo pali waung’ono ndi wina wochepetsetsa.
Machimo akuluakulu ali ngati awa: (a) Kuphatikiza Allah ndi mafano. (b) Kupha munthu wosalakwa. (c) Kuba. (d) Kuchita malonda akatapira (riba). (e) Kumwa zoledzeretsa. (f) Kuchita chiwerewere ndi zina zotero.
Tsono uchimo waung’ono uli monga: Kunena mawu osafunika ndi kuchiyang’ana chinthu choletsedwa ndi zina zotero zomwe nzovuta munthu kuzipewa. Choncho, munthu akapewa machimo akuluakulu ndiye kuti adzamkhululukira machimo ang’onoang’ono ngati sakuwachita mochulukitsa.
Enanso mwa machimo akuluakulu ndikusiya kutsata malamulo a Allah, monga (a) Kusiya kupemphera Swala zisanu. (b) Kusiya kupereka Zakaat ndi zithandizo zina zofunika. (c) Kusiya kumanga m’mwezi wa Ramadan. (d) Kusiya kuchita Hajj. (e) Kusiya kuyang’anira makolo ndi zina zotero.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (31) Surah: Soerat An-nisa (de vrouwen)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit