Check out the new design

Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: El-Maidah   Vers:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمۡ تَعَالَوۡاْ إِلَىٰ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ وَإِلَى ٱلرَّسُولِ قَالُواْ حَسۡبُنَا مَا وَجَدۡنَا عَلَيۡهِ ءَابَآءَنَآۚ أَوَلَوۡ كَانَ ءَابَآؤُهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ شَيۡـٔٗا وَلَا يَهۡتَدُونَ
Ndipo akauzidwa: “Tadzani kuchilamulo cha zomwe Allah wavumbulutsa ndi (zomwe akunena) Mtumiki.” Akunena: “Tikukwaniritsidwa ndi zomwe tidawapeza nazo makolo athu.” Kodi ngakhale kuti makolo awowo sadali kudziwa chinthu chilichonse ndipo sadali oongoka, (awatsatirabe)?
Arabische uitleg van de Qur'an:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ عَلَيۡكُمۡ أَنفُسَكُمۡۖ لَا يَضُرُّكُم مَّن ضَلَّ إِذَا ٱهۡتَدَيۡتُمۡۚ إِلَى ٱللَّهِ مَرۡجِعُكُمۡ جَمِيعٗا فَيُنَبِّئُكُم بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Dziganizireni nokha. Ndipo amene asokera sangakupatseni mavuto ngati inu mutalungama. Nonsenu kobwerera kwanu nkwa Allah basi. Choncho adzakuuzani zimene mudali kuchita.
Arabische uitleg van de Qur'an:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ شَهَٰدَةُ بَيۡنِكُمۡ إِذَا حَضَرَ أَحَدَكُمُ ٱلۡمَوۡتُ حِينَ ٱلۡوَصِيَّةِ ٱثۡنَانِ ذَوَا عَدۡلٖ مِّنكُمۡ أَوۡ ءَاخَرَانِ مِنۡ غَيۡرِكُمۡ إِنۡ أَنتُمۡ ضَرَبۡتُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَأَصَٰبَتۡكُم مُّصِيبَةُ ٱلۡمَوۡتِۚ تَحۡبِسُونَهُمَا مِنۢ بَعۡدِ ٱلصَّلَوٰةِ فَيُقۡسِمَانِ بِٱللَّهِ إِنِ ٱرۡتَبۡتُمۡ لَا نَشۡتَرِي بِهِۦ ثَمَنٗا وَلَوۡ كَانَ ذَا قُرۡبَىٰ وَلَا نَكۡتُمُ شَهَٰدَةَ ٱللَّهِ إِنَّآ إِذٗا لَّمِنَ ٱلۡأٓثِمِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Pamene chamfikira mmodzi wa inu chisonyezo cha imfa, ndipo akufuna kusiya chilawo (wasiya) funani mboni ponena mawuwo. Aikire umboni awiri olungama mwa inu (Asilamu) kapena apadera ngati muli pa ulendo, ndipo zisonyezo za imfa zitaonekera. Ngati mutazikaikira zitsekerezeni (kuti zisachoke) mboni ziwiri pambuyo pa Swala (yomwe amasonkhana anthu ambiri), ndipo zilumbilire m’dzina la Allah kunena (kuti): “Sitikusinthanitsa malumbirowa ndi china chake ngakhale chitakhala chothandiza kwa ife kapena mmodzi mwa abale athu. Sitikubisa umboni umene Allah watilamula kuti tiupereke moona. Ife ngati titabisa umboni (kapena kuyankhula chonama), ndithudi tikhala mwa anthu ochimwa.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَإِنۡ عُثِرَ عَلَىٰٓ أَنَّهُمَا ٱسۡتَحَقَّآ إِثۡمٗا فَـَٔاخَرَانِ يَقُومَانِ مَقَامَهُمَا مِنَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَحَقَّ عَلَيۡهِمُ ٱلۡأَوۡلَيَٰنِ فَيُقۡسِمَانِ بِٱللَّهِ لَشَهَٰدَتُنَآ أَحَقُّ مِن شَهَٰدَتِهِمَا وَمَا ٱعۡتَدَيۡنَآ إِنَّآ إِذٗا لَّمِنَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Koma ngati kutaoneka kuti mboni ziwiri zija zanama pa umboni wawo, kapena zabisa chinthu, apo awiri achibale a wakufayo aimiire m’malo mwa mboni ziwirizo, (pambuyo pa Swala kuti aulule za bodza lawo). Choncho alumbilire m’dzina la Allah kuti: “Ndithu kulumbira kwathu nkoyenera kuvomerezedwa kuposa kulumbira kwawo; ndipo sitinapyole malire (mukulumbira kwathu). Ndipo sitikuzipekera mbonizo bodza. Ndithudi, ngati ife titachita zotere, ndiye kuti tikhala mwa ochita zoipa, (oyenera kulandira chilango cha Allah).”
Arabische uitleg van de Qur'an:
ذَٰلِكَ أَدۡنَىٰٓ أَن يَأۡتُواْ بِٱلشَّهَٰدَةِ عَلَىٰ وَجۡهِهَآ أَوۡ يَخَافُوٓاْ أَن تُرَدَّ أَيۡمَٰنُۢ بَعۡدَ أَيۡمَٰنِهِمۡۗ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱسۡمَعُواْۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
Chilamulochi ndi njira yapafupi kuti mboni zikwaniritse umboni wawo mnjira yoyenera, (ndikuti zisamalire kulumbira Allah kwawo); kapena kuopa kuyaluka bodza lawo likaonekera poyera, pambuyo polumbira enawo (izi zili polumbira amlowa mmalo pokana umboni wawo). Ndipo opani Allah (mkulumbira kwanu ndi kukhulupirika kwanu), ndipo mverani malamulo Ake. Allah satsogolera anthu opandukira chilamulo Chake.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: El-Maidah
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chichewa-vertaling - Khalid Ibrahim Beitala - Index van vertaling

Vertaald door Khalid Ibrahim Bitala.

Sluit