Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (17) Surah: Soerat El-Maidah (De tafel)
لَّقَدۡ كَفَرَ ٱلَّذِينَ قَالُوٓاْ إِنَّ ٱللَّهَ هُوَ ٱلۡمَسِيحُ ٱبۡنُ مَرۡيَمَۚ قُلۡ فَمَن يَمۡلِكُ مِنَ ٱللَّهِ شَيۡـًٔا إِنۡ أَرَادَ أَن يُهۡلِكَ ٱلۡمَسِيحَ ٱبۡنَ مَرۡيَمَ وَأُمَّهُۥ وَمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗاۗ وَلِلَّهِ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَاۚ يَخۡلُقُ مَا يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Ndithudi, amukana (Allah) amene akunena kuti Mulungu ndiye Mesiya Mwana wa Mariya. Nena: “Ndani akadatha kuletsa chilichonse kwa Allah ngati Iye akadafuna kuononga Mesiya mwana wa Mariya ndi mayi wakeyo, ndi onse omwe ali m’dziko lapansi? Ndipo ufumu wa kumwamba ndi pansi ndi zapakati pake ngwa Allah. Amalenga chimene wafuna. Ndipo Allah Ngokhoza chilichonse.”[161]
[161] Mndime iyi atchula zoyankhula zawo za machimo zoti Isa (Yesu) ndi mwana wa Mulungu, kapena ndi Mulungu amene, kapena ndi mmodzi mmilungu itatu. Ndipo akunenetsa za kufooka kwa mneneri Isa (Yesu) pamaso pa Allah monga kulili kufookanso kwa zolengedwa zina.
Ndimeyi ikunenetsanso kuti Allah monga amalenga mkalengedwe kamene Iye wafuna, mchosadabwitsa kwa Iye kulenga Isa (Yesu) popanda tate. Ndipo nchosadabwitsanso kwa Iye kulenga Adam popanda tate ndi mayi. Nanga nchotani kuti Akhrisitu azimuyesa Mneneri Isa (Yesu) kuti ndi mwana wa Mulungu kamba koti alibe tate? Bwanji nanga Adam naye sakumuyesa mwana wa Mulungu poti nayenso alibe tate ndi mayi? Ndibwino kutsata choonadi ngakhale choonadicho chikuchokera kwa mdani. Choonadi ndi choonadi.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (17) Surah: Soerat El-Maidah (De tafel)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit