Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Monaafiqoen (De Huichelaars)   Vers:

Soerat Al-Monaafiqoen (De Huichelaars)

إِذَا جَآءَكَ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ قَالُواْ نَشۡهَدُ إِنَّكَ لَرَسُولُ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ إِنَّكَ لَرَسُولُهُۥ وَٱللَّهُ يَشۡهَدُ إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ لَكَٰذِبُونَ
Akakudzera achiphamaso akunena kuti: “Tikuikira umboni kuti ndithu iwe ndiwe Mtumiki wa Allah, ndipo Allah akudziwa kuti iwe ndiwe mtumiki Wake. Ndipo Allah akuikira umboni kuti achiphamaso ngabodza (pa zomwe akunena).
Arabische uitleg van de Qur'an:
ٱتَّخَذُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُمۡ جُنَّةٗ فَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۚ إِنَّهُمۡ سَآءَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Kulumbira kwawo (kwa bodza) akuchita kukhala chotetezera (chuma chawo ndi matupi awo). Tero atsekereza (anthu kuyenda) panjira ya Allah. Ndithu nzoipa zedi zimene amachita.
Arabische uitleg van de Qur'an:
ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ ءَامَنُواْ ثُمَّ كَفَرُواْ فَطُبِعَ عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ فَهُمۡ لَا يَفۡقَهُونَ
Zimenezo nchifukwa chakuti iwo adakhulupirira (modzionetsera), kenako adakana (mobisa). Choncho mitima yawo idatsekedwa kotero kuti iwo sangathe kuzindikira (chimene chingawapulumutse ku chilango cha Allah.)
Arabische uitleg van de Qur'an:
۞ وَإِذَا رَأَيۡتَهُمۡ تُعۡجِبُكَ أَجۡسَامُهُمۡۖ وَإِن يَقُولُواْ تَسۡمَعۡ لِقَوۡلِهِمۡۖ كَأَنَّهُمۡ خُشُبٞ مُّسَنَّدَةٞۖ يَحۡسَبُونَ كُلَّ صَيۡحَةٍ عَلَيۡهِمۡۚ هُمُ ٱلۡعَدُوُّ فَٱحۡذَرۡهُمۡۚ قَٰتَلَهُمُ ٱللَّهُۖ أَنَّىٰ يُؤۡفَكُونَ
Ndipo ukawaona, akukondweretsa matupi awo; ndipo akayankhula umvetsera zoyankhula zawo (chifukwa chakuthwa kwa malirime awo, pomwe mkati mwawo ndiming’oma yopanda kanthu); iwo ali ngati matsinde a mitengo yomwe yayadzamiritsidwa (ku chipupa); (mwa iwo mulibe moyo). Mkuwe uliwonse (umene akuumva) akuganiza kuti ukulinga iwo, (chifukwa cha kuzindikira chinyengo chawo); iwowa ndiadani; chenjerani nawo. Allah awatembelere! Mwanjira yanji akuchotsedwa (ku choonadi)!
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمۡ تَعَالَوۡاْ يَسۡتَغۡفِرۡ لَكُمۡ رَسُولُ ٱللَّهِ لَوَّوۡاْ رُءُوسَهُمۡ وَرَأَيۡتَهُمۡ يَصُدُّونَ وَهُم مُّسۡتَكۡبِرُونَ
Kukanenedwa kwa iwo kuti: “Bwerani, akupemphereni chikhululuko mthenga wa Allah, akutembenuza mitu yawo (monyoza ndi modzitukumula), ndipo uwaona akunyoza uku akudzikweza (osatsatira langizo).”
Arabische uitleg van de Qur'an:
سَوَآءٌ عَلَيۡهِمۡ أَسۡتَغۡفَرۡتَ لَهُمۡ أَمۡ لَمۡ تَسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ لَن يَغۡفِرَ ٱللَّهُ لَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
Kwa iwowa nchimodzimodzi kuwapemphera kwako chikhululuko, kapena kusawapemphera. Allah sangawakhululukire (chifukwa cha kuzama kwawo m’kusakhulupirira). Ndithu Allah saongola anthu otuluka m’chilamulo (Chake).
Arabische uitleg van de Qur'an:
هُمُ ٱلَّذِينَ يَقُولُونَ لَا تُنفِقُواْ عَلَىٰ مَنۡ عِندَ رَسُولِ ٱللَّهِ حَتَّىٰ يَنفَضُّواْۗ وَلِلَّهِ خَزَآئِنُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَلَٰكِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ لَا يَفۡقَهُونَ
Amenewa ndiwo omwe akunena kwa Answari; (Asilamu aku Madina, kuti): “Musawapatse chuma (chanu) amene ali ndi Mtumiki wa Allah kuti abalalikane.” Pomwe nkhokwe zonse (zachuma) za kumwamba ndi dziko lapansi zili m’manja mwa Allah (ndipo amachipereka kwa amene wamfuna); koma achiphamaso sakuzindikira (zimenezo).[364]
[364] (Ndime 7-8) Chifukwa chomwe ndime izi zidavumbulutsidwira ndi kuti tsiku lina Mtumiki (s.a.w) pomwe adali ndi gulu lake la nkhondo, munthu wina wa m’madera am’midzi adakangana ndi Msilamu wa mu mzinda wa Madina chifukwa cha madzi. Ndipo Mwarabu wa kumudzi uja adamenya Msilamu wa m’Madina ndi thabwa. Poona izi Msilamu wa ku Madina adapita kukasuma kwa mwana wa Ubayye amene adali munafiki (wachinyengo). Mwana wa Ubayyeyo adamuuza wosumayo kuti: “Musamawapatse chakudya omwe ali ndi Muhammad kuti abalalikane, athawe njala ndi kumsiya yekha Muhammad (s.a.w).” Adatinso: “Tikabwerera ku mzinda wa Madina, wolemekezeka adzatulutsa wonyozeka.” Apa amatanthauza kuti wolemekezeka ndiye iye, ndipo wonyozeka ndi Mtumiki Muhammad (s.a.w). Ndipo Allah adamuyankha ponena kuti: “Kulemekezeka ndi kwa Allah ndi Mthenga wake ndi okhulupilira; koma anthu achiphamaso sakudziwa zimenezi.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
يَقُولُونَ لَئِن رَّجَعۡنَآ إِلَى ٱلۡمَدِينَةِ لَيُخۡرِجَنَّ ٱلۡأَعَزُّ مِنۡهَا ٱلۡأَذَلَّۚ وَلِلَّهِ ٱلۡعِزَّةُ وَلِرَسُولِهِۦ وَلِلۡمُؤۡمِنِينَ وَلَٰكِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ لَا يَعۡلَمُونَ
Akunena kuti: “Ngati tibwerera ku Madina wolemekezeka adzatulutsa wonyozeka m’menemo. “Pomwe ulemelero ngwa Allah ndi Mthenga Wake ndi okhulupirira; koma achinyengo sakudziwa (zimenezo).”
Arabische uitleg van de Qur'an:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تُلۡهِكُمۡ أَمۡوَٰلُكُمۡ وَلَآ أَوۡلَٰدُكُمۡ عَن ذِكۡرِ ٱللَّهِۚ وَمَن يَفۡعَلۡ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Chuma chanu ngakhalenso ana anu zisakutangwanitseni ndi kusiya kukumbukira Allah (ndi kukwaniritsa zimene wakulamulani). Ndipo amene achite zimenezo iwo ndi otaika.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَأَنفِقُواْ مِن مَّا رَزَقۡنَٰكُم مِّن قَبۡلِ أَن يَأۡتِيَ أَحَدَكُمُ ٱلۡمَوۡتُ فَيَقُولَ رَبِّ لَوۡلَآ أَخَّرۡتَنِيٓ إِلَىٰٓ أَجَلٖ قَرِيبٖ فَأَصَّدَّقَ وَأَكُن مِّنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Perekani (mwachangu pa njira ya Allah) zina mwa zomwe takupatsani, isanamfikire mmodzi wa inu imfa (mwadzidzidzi) ndi kuyamba kunena (modandaula): “Mbuye wanga! Bwanji osandichedwetsa nthawi pang’ono kuti ndipereke sadaka (ndi kuti ndikonze zina zimene sindinazikwaniritse) ndi kutinso ndikhale mwa anthu anu abwino.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَن يُؤَخِّرَ ٱللَّهُ نَفۡسًا إِذَا جَآءَ أَجَلُهَاۚ وَٱللَّهُ خَبِيرُۢ بِمَا تَعۡمَلُونَ
Ndipo Allah sangauchedwetse mzimu (ngakhale ndi mphindi imodzi) ukaidzera nthawi yake ya imfa; ndipo Allah Ngodziwa zonse zimene mukuchita, (ndipo adzakulipirani pa zimenezo).
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Monaafiqoen (De Huichelaars)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit