Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (38) Surah: Soerat el-Araf (De verheven plaatsen)
قَالَ ٱدۡخُلُواْ فِيٓ أُمَمٖ قَدۡ خَلَتۡ مِن قَبۡلِكُم مِّنَ ٱلۡجِنِّ وَٱلۡإِنسِ فِي ٱلنَّارِۖ كُلَّمَا دَخَلَتۡ أُمَّةٞ لَّعَنَتۡ أُخۡتَهَاۖ حَتَّىٰٓ إِذَا ٱدَّارَكُواْ فِيهَا جَمِيعٗا قَالَتۡ أُخۡرَىٰهُمۡ لِأُولَىٰهُمۡ رَبَّنَا هَٰٓؤُلَآءِ أَضَلُّونَا فَـَٔاتِهِمۡ عَذَابٗا ضِعۡفٗا مِّنَ ٱلنَّارِۖ قَالَ لِكُلّٖ ضِعۡفٞ وَلَٰكِن لَّا تَعۡلَمُونَ
(Allah) adzati (pa tsiku la chiweruziro): “Lowani ku Moto pamodzi ndi mibadwo imene idamuka kale (inu musanabwere) yochokera m’ziwanda ndi mu anthu. M’badwo uliwonse pamene uzikalowa, udzatembelera unzake, kufikira pamene onse adzasonkhana m’menemo. Adzanena apambuyo kwa oyambilira awo: “Mbuye wathu! Awa, adatisokeretsa. Apatseni chilango cha Moto chochuluka.” (Allah) adzanena: “Aliyense mwa inu akhala ndi chilango chochuluka; koma izi inu simukudziwa.”[183]
[183] Aliyense adzapeza chilango chachikulu. Ndipo awo amene adasokeretsedwa: (a) Adzapeza chilango chifukwa cholola kusokeretsedwa pomwe adapatsidwa nzeru zowazindikiritsa zabwino ndi zoipa. (b) Adzapeza chilango chifukwa chochita machimowo. Tsono amene adali kusokeretsa anzawo:
a) Adzapeza chilango chifukwa chakuchita kwawo machimo.
b) Adzapeza chilango chifukwa chakuwasokeretsa anthu omwe adawasokeretsa.
c) Adzapeza chilango chifukwa chakuyambitsa machimowo.
d) Adzapeza chilango chifukwa chowasiira anzawo odza m’mbuyo mwawo machimo powatsanzira iwo.
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (38) Surah: Soerat el-Araf (De verheven plaatsen)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit