Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (60) Surah: Soerat at-Tauba (Berouw)
۞ إِنَّمَا ٱلصَّدَقَٰتُ لِلۡفُقَرَآءِ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَٱلۡعَٰمِلِينَ عَلَيۡهَا وَٱلۡمُؤَلَّفَةِ قُلُوبُهُمۡ وَفِي ٱلرِّقَابِ وَٱلۡغَٰرِمِينَ وَفِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَٱبۡنِ ٱلسَّبِيلِۖ فَرِيضَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
Ndithu sadaka (za Zakaati) ndi za mafukara, masikini, ogwira ntchito yosonkhetsa sadakazo, owalimbitsa mitima yawo (pa Chisilamu amene alowa kumene), kuombolera akapolo (kuti akhale afulu), kuthandizira amene ali m’ngongole; kuzipereka pa njira ya Allah; ndi kuwapatsa a paulendo (omwe alibe choyendera). Ili ndi lamulo lochokera kwa Allah, ndipo Allah Ngodziwa kwabasi, Ngwanzeru zakuya.[211]
[211] M’ndime iyi Allah akutifotokozera magulu a anthu amene ngoyenera kuwagawira chuma cha Zakaat. Iwo ndi awa:- 1. Osauka amene sangagwire ntchito nkudzipezera okha chakudya (mafukara). 2. Osauka amene alibe zokwanira pa zofunikira pa moyo wawo (Masikini). 3. Amene akusonkhetsa chuma cha Zakaat cho omwe ntchito yawo ndiyokhayo. 4. Amene angolowa kumene m’Chisilamu omwe akuyembekezedwa kuti akapatsidwa adzalimbikitsidwa mitima yawo pa chipembedzochi. 5. Amene afuna kudziombola ku ukapolo. 6. Amene akulephera kulipira ngongole ya choonadi. 7. Amene akuchita Jihâd panjira ya Allah. 8. Wapaulendo amene alibe choyendera (ndalama zoyendera).
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (60) Surah: Soerat at-Tauba (Berouw)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit