Check out the new design

د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه سورت: نحل   آیت:
وَتَحۡمِلُ أَثۡقَالَكُمۡ إِلَىٰ بَلَدٖ لَّمۡ تَكُونُواْ بَٰلِغِيهِ إِلَّا بِشِقِّ ٱلۡأَنفُسِۚ إِنَّ رَبَّكُمۡ لَرَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Ndipo zimasenza mitolo yanu (yolemera) kukafika nayo ku midzi yakutali komwe simumatha kukafikako popanda kuvutika kwambiri. Ndithu Mbuye wanu Ngodekha kwabasi, Ngwachisoni zedi.
عربي تفسیرونه:
وَٱلۡخَيۡلَ وَٱلۡبِغَالَ وَٱلۡحَمِيرَ لِتَرۡكَبُوهَا وَزِينَةٗۚ وَيَخۡلُقُ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
(Adalenganso) akavalo, nyumbu ndi abulu kuti muzizikwera ndi kutinso zizikhala chokometsera chanu (cholowetsa chisangalalo m’mitima yanu); ndipo adzalenga (zokwera zina) zomwe simukuzidziwa.
عربي تفسیرونه:
وَعَلَى ٱللَّهِ قَصۡدُ ٱلسَّبِيلِ وَمِنۡهَا جَآئِرٞۚ وَلَوۡ شَآءَ لَهَدَىٰكُمۡ أَجۡمَعِينَ
Ndipo ndi udindo wa Allah kusonyeza njira yolungama (yomwe ingakufikitseni ku Munda wamtendere), koma zilipo njira zina zokhota (zomwe sizifikitsa ku choonadi). Ndipo Allah akadafuna, akadakuongolani nonsenu (mwa chifuniro chanu ndi mopanda chifuniro chanu. Koma Iye adakupatsani nzeru kuti musankhe nokha njira imene mufuna).
عربي تفسیرونه:
هُوَ ٱلَّذِيٓ أَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗۖ لَّكُم مِّنۡهُ شَرَابٞ وَمِنۡهُ شَجَرٞ فِيهِ تُسِيمُونَ
Iye ndi Amene akukutsitsirani madzi kuchokera ku mitambo, madziwo mumamwa (pothetsa ludzu lanu), ndipo ndi madziwo mitengo imamera; mitengo yomwe mumadyetsera ziweto (zanu).
عربي تفسیرونه:
يُنۢبِتُ لَكُم بِهِ ٱلزَّرۡعَ وَٱلزَّيۡتُونَ وَٱلنَّخِيلَ وَٱلۡأَعۡنَٰبَ وَمِن كُلِّ ٱلثَّمَرَٰتِۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لِّقَوۡمٖ يَتَفَكَّرُونَ
Ndi madzi omwewo amakumeretserani mmera, (mitengo ya) mzitona, kanjedza, mphesa, ndi mitundu ina yonse ya zipatso. Ndithu kupezeka kwa zimenezi ndi chisonyezo (chosonyeza mphamvu za Allah) kwa anthu olingalira.[248]
[248] Ndithudi, m’kutsika kwa madzi kuchokera ku mitambo ndi kumeretsa zipatso, muli zisonyezo zoonekera poyera kukhoza kwa Allah ndi umodzi wake kwa anthu omwe amalingalira za zolengedwa Zake. Ndipo potero amakhulupilira Allah Kodi simukuona mbewu imodzi ikaikidwa m’nthaka ndi kupitapo nyengo yodziwika, imafunafuna potulukira ndi kung’amba nthaka ndi kukula kusanduka mtengo? Zonsezi nzododometsa kwa anthu olingalira.
عربي تفسیرونه:
وَسَخَّرَ لَكُمُ ٱلَّيۡلَ وَٱلنَّهَارَ وَٱلشَّمۡسَ وَٱلۡقَمَرَۖ وَٱلنُّجُومُ مُسَخَّرَٰتُۢ بِأَمۡرِهِۦٓۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَٰتٖ لِّقَوۡمٖ يَعۡقِلُونَ
Ndipo chifukwa cha inu adagonjetsa usiku ndi usana; dzuwa ndi mwezi; (zonse zidalengedwa kuti zibwere ndi zokomera inu). Nazo nyenyezi zidagonjetsedwa mwa lamulo Lake. Ndithu m’zimenezi muli zizindikiro kwa anthu anzeru.
عربي تفسیرونه:
وَمَا ذَرَأَ لَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُخۡتَلِفًا أَلۡوَٰنُهُۥٓۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لِّقَوۡمٖ يَذَّكَّرُونَ
Ndiponso ndi zimene adakulengerani m’nthaka (zinthu zododornetsa monga nyama, mmera, miyala yamtengo wapatali, zamoyo ndi zopanda moyo), zautoto wosiyanasiyana ndi maonekedwe osiyanasiyana; ndithu m’zimenezo muli zisonyezo kwa anthu olalikika.
عربي تفسیرونه:
وَهُوَ ٱلَّذِي سَخَّرَ ٱلۡبَحۡرَ لِتَأۡكُلُواْ مِنۡهُ لَحۡمٗا طَرِيّٗا وَتَسۡتَخۡرِجُواْ مِنۡهُ حِلۡيَةٗ تَلۡبَسُونَهَاۖ وَتَرَى ٱلۡفُلۡكَ مَوَاخِرَ فِيهِ وَلِتَبۡتَغُواْ مِن فَضۡلِهِۦ وَلَعَلَّكُمۡ تَشۡكُرُونَ
Ndipo Iye ndi Yemwe adagonjetsa nyanja kuti mudye nyama yamatumbi (ya) m’menemo (nsomba) ndikuti mutulutse m’menemo zodzikongoletsera zomwe mumavala; ndipo uona zombo zikuluzikulu zikung’amba (mafunde) m’menemo kuti mufunefune zabwino zake (njira ya malonda), ndi kuti muthokoze (Mbuye wanu Allah).
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه سورت: نحل
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا - د ژباړو فهرست (لړلیک)

خالد إبراهيم بيتالا ژباړلی دی.

بندول