د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه آیت: (44) سورت: النساء
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ نَصِيبٗا مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِ يَشۡتَرُونَ ٱلضَّلَٰلَةَ وَيُرِيدُونَ أَن تَضِلُّواْ ٱلسَّبِيلَ
Kodi sukuwaona omwe adapatsidwa gawo la (nzeru zozindikira) buku (la Allah, omwe ndi Ayuda ndi Akhrisitu), akudzisankhira kusokera ndiponso akufuna mutasokera kusiya njira (yabwino).[125]
[125] (Ndime 44-46) Apa akutchula kuipa kwina kwa Ayuda ndi Akhrisitu. Iwo adali kusintha mawu omwe adali m’mabuku a Taurat ndi Injil, makamaka mawu amene adali kusonyeza za uneneri wa Muhammad (s.a.w). Kapena adali kuwatanthauzira m’njira zina zogwirizana ndi zolinga zawo. Pamene adali kudza kwa Mtumiki Muhammad (s.a.w) makamaka Ayuda, akawalalikira mawu achipembedzo, ankati: “Tamva, titsatira,” pomwe m’mitima mwawo akuti “Sititsatira zonse zomwe ukunena. Koma tikungokunyenga chabe.” Amati akadza nkumva momwe maswahaba amanenera ndi Mtumiki (s.a.w), Mtumiki akawalalikira, amati: “Ismaa ghayra musma’” monga mwa chizolowezi cha Arabu akauzidwa mawu ofunika. Tanthuzo lake nkuti, “Imva siumvanso choipa kuchokera kwa ife ngati Allah afuna.” Naonso Ayuda adali kumnenera Mtumiki mawu omwewa, koma m’mitima mwawo akulinga tanthauzo lina. M’mitima mwawo amalinga kuti, “Siumva zabwino kuchokera kwa ife ngati Allah afuna, koma zokusowetsa mtendere zokhazokha.” Ndipo amati akabweranso Ayudawo nkumva maswahaba akumuuza Mtumiki kuti; “Raa’ina”. Kutanthauza kuti, “Tiyang’ane ndi diso lachifundo,” iwonso amayankhula mawu omwewa, koma mokhotetsa pang’ono mpaka kusinthika tanthauzo lake. M’chiyankhulo cha chiyuda limatanthauza kuti “E iwe mbutuma!” Ndipo iwo m’kunena kwawo amalinga tanthauzo limeneli. Choncho Asilamu anawauza kuti azigwiritsira ntchito mawu oti “Undhurna.” Ndipo mawuwa tanthauzo lake ndilofanana. Koma mawu awa Ayuda sakadatha kuwakhotetsa.
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه آیت: (44) سورت: النساء
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - د ژباړو فهرست (لړلیک)

چیچوایي ژبې ته د قرآن کریم د معناګانو ژباړه، خالد ابراهیم بیتالا ژباړلې ده، ۲۰۲۰ کال چاپ

بندول