د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه آیت: (2) سورت: الجمعة
هُوَ ٱلَّذِي بَعَثَ فِي ٱلۡأُمِّيِّـۧنَ رَسُولٗا مِّنۡهُمۡ يَتۡلُواْ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتِهِۦ وَيُزَكِّيهِمۡ وَيُعَلِّمُهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَإِن كَانُواْ مِن قَبۡلُ لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ
Iye ndiAmene adatumiza kwa Ummiyyina (osadziwa kulemba ndi kuwerenga), Mtumiki wochokera mwa iwo kuti awawerengere ndime Zake ndi kuti awayeretse (ku uchimo ndi kumakhalidwe oipa) ndi kuwaphunzitsa Qur’an ndi mawu anzeru (a mtumiki) ndithu kale adali osokera kowonekera (Mtumiki {s.a.w} asadadze kwa iwo).[361]
[361] Arabu amatchedwa “Ummiyyuna” chifukwa chakuti samadziwa kulemba ndi kuwerenga. Kusadziwa kulemba ndi kuwerenga kudafala pakati pawo ndipo ngakhale Mtumiki amene samadziwa kulemba ndi kuwerenga chilichonse. M’ndime imeneyi, Allah akutiphunzitsa kuti adampereka Muhammad (s.a.w) kuti awaongolere anthu ku njira yoongoka. Iyeyu adaperekedwa panyengo imene anthu adali ndi khumbo la Mneneri wa Allah kuti awatsogolere ku njira yolungama pakuti pa nthawiyo zipembedzo zonse za Allah zidali zitaonongeka. Pachiyambi Arabu amatsatira chipembedzo cha Ibrahim. Kenako adasintha nkuyamba kupembedza mafano. Adayambitsa zinthu zambiri zosalolezedwa ndi Allah. Ndipo nawonso anthu amabuku, Ayuda ndi Akhrisitu, adasintha zophunzitsa za mabuku awo. Choncho Allah adapereka Muhammad (s.a.w) ndi malamulo aakulu okwanira bwino. Mkati mwake mudali chilichonse chofunika m’moyo wa anthu pa nyengo zosiyanasiyana pa moyo wa pa dziko ndi wa pa tsiku lachimaliziro. Allah adampatsa zabwino zomwe sadampatseponso wina aliyense, woyamba ndi womaliza.
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه آیت: (2) سورت: الجمعة
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - د ژباړو فهرست (لړلیک)

چیچوایي ژبې ته د قرآن کریم د معناګانو ژباړه، خالد ابراهیم بیتالا ژباړلې ده، ۲۰۲۰ کال چاپ

بندول