Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Versículo: (10) Surah: Suratu Luqman
خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ بِغَيۡرِ عَمَدٖ تَرَوۡنَهَاۖ وَأَلۡقَىٰ فِي ٱلۡأَرۡضِ رَوَٰسِيَ أَن تَمِيدَ بِكُمۡ وَبَثَّ فِيهَا مِن كُلِّ دَآبَّةٖۚ وَأَنزَلۡنَا مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَنۢبَتۡنَا فِيهَا مِن كُلِّ زَوۡجٖ كَرِيمٍ
Adalenga thambo popanda mizati yomwe mukuiona. Ndipo adaika mapiri m’nthaka kuti isakugwedezeni. Ndipo (Iye) adafalitsa nyama m’menemo zamitundu yosiyanasiyana. Ndipo tidatsitsa madzi kuchokera ku mitambo, choncho tidameretsa m’menemo (m’nthaka) mmera wokongola wamitundu yosiyanasiyana.[311]
[311] M’ndime iyi Allah akutifotokozera kuti adalenga thambo monga lilili m’kukula kwake ndi m’kuphanuka kwake ndi kulimba kwake popanda mizati yolichirikiza. Ndipo inu anthu mukuliona mmene lili lopanda chilichonse choligwira koma mphamvu za Allah Wamkulu Wapamwambamwamba.
Ndipo m’nthaka adaikamo mapiri akuluakulu kuti nthaka isamagwedezeke ndi kumakusowetsani mtendere, kapena kumakugumulirani nyumba zanu. Ndipo Allah adafalitsa padziko zamoyo zochuluka ndi kumeretsa mbewu zosiyanasiyana. Zonsezi zikusonyeza mphamvu Zake zoopsa.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Versículo: (10) Surah: Suratu Luqman
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar