Check out the new design

Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro bya Qur'an Ntagatifu mu rurimi rw'igi Chewa - Khaled Ibrahim Betala. * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Isura: Al An’fal   Umurongo:
إِذۡ تَسۡتَغِيثُونَ رَبَّكُمۡ فَٱسۡتَجَابَ لَكُمۡ أَنِّي مُمِدُّكُم بِأَلۡفٖ مِّنَ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ مُرۡدِفِينَ
(Kumbukirani) pamene mudali kupempha Mbuye wanu chithandizo, ndipo anakuyankhani kuti: “Ndithudi, Ine ndikuthandizani ndi chikwi cha angelo otsatizana potsika, (omenya nkhondo).”
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَمَا جَعَلَهُ ٱللَّهُ إِلَّا بُشۡرَىٰ وَلِتَطۡمَئِنَّ بِهِۦ قُلُوبُكُمۡۚ وَمَا ٱلنَّصۡرُ إِلَّا مِنۡ عِندِ ٱللَّهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٌ
Ndipo Allah sadachite ichi koma kuti chikhale nkhani yabwino (yosangalatsa), ndi kuti mitima yanu ikhazikike ndi chimenecho. Ndipo palibe chipulumutso (chothandiza) koma chimene chachokera kwa Allah. Ndithu Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.[192]
[192] (Ndime 10-11) Asilamu adapeza lonjezo lochoka kwa Allah lakuti pa nthawi ya nkhondo adzawatumizira angelo, pamenepo mitima ya Asilamu idakhazikika kotero kuti ena mwa iwo adadzilotera nakhala ndi Janaba. Choncho panafunika kuti asambe, koma madzi panalibe. Ndipo mwadzidzidzi mvula idawavumbwira ndipo adapeza madzi osamba ndi ena ogwira nawo ntchito zina. Chigwa cha Badiri chidali chamchenga wokhawokha. Ndipo mchenga umene udali kumbali ya Asilamu udali wosayendeka. Munthu akati ayende, mapazi amangozama. Tero pamene mvulayo idavumbwa, mchengawo udagwirana nkukhala woyendeka. Zitatero Asilamu zidawayendera bwino. Koma kumbali ya Amushirikina kudali matope okhaokha. Choncho sadathe kuyenda mwachangu. Umo ndimomwe chifundo cha Allah chidalili pa Asilamu.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِذۡ يُغَشِّيكُمُ ٱلنُّعَاسَ أَمَنَةٗ مِّنۡهُ وَيُنَزِّلُ عَلَيۡكُم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ لِّيُطَهِّرَكُم بِهِۦ وَيُذۡهِبَ عَنكُمۡ رِجۡزَ ٱلشَّيۡطَٰنِ وَلِيَرۡبِطَ عَلَىٰ قُلُوبِكُمۡ وَيُثَبِّتَ بِهِ ٱلۡأَقۡدَامَ
(Kumbukirani) pamene anakugonetsani tulo tomwe tidali mtendere wochokera kwa Iye, ndipo anavumbwitsa mvula pa inu yochokera ku mitambo kuti akuyeretseni nayo (matupi anu) ndikukuchotserani manong’onong’o a satana, ndi kuipatsa mphamvu mitima yanu ndiponso ndi kulimbikitsa mapazi anu (pamchenga).
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِذۡ يُوحِي رَبُّكَ إِلَى ٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ أَنِّي مَعَكُمۡ فَثَبِّتُواْ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْۚ سَأُلۡقِي فِي قُلُوبِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ ٱلرُّعۡبَ فَٱضۡرِبُواْ فَوۡقَ ٱلۡأَعۡنَاقِ وَٱضۡرِبُواْ مِنۡهُمۡ كُلَّ بَنَانٖ
(Kumbukira) pamene Mbuye wako anawauza angelo kuti: “Ine ndili pamodzi nanu (pokulimbikitsani ndi chithandizo Changa). Alimbikitseni amene akhulupirira, ndipo ndidzathira mantha mmitima mwa amene sadakhulupirire. Choncho amenyeni mmwamba mwa makosi awo, ndi kuwadula nsonga za zala zawo (zimene akugwilira zida).
Ibisobanuro by'icyarabu:
ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ شَآقُّواْ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥۚ وَمَن يُشَاقِقِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَإِنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
Izi ndi chifukwa chakuti iwo anatsutsana ndi Allah ndi Mtumiki wake (iwo podziika mbali ina kusiya komwe kudali Allah). Amene anatsutsana ndi Allah ndi Mtumiki Wake, ndithu Allah ndi wolanga kwambiri (amalanga ndi chilango choopsa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
ذَٰلِكُمۡ فَذُوقُوهُ وَأَنَّ لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابَ ٱلنَّارِ
Chimenecho ndi chilango (cha Allah E inu Maquraish)! Choncho chilaweni. Ndithu osakhulupirira adzapeza chilango cha Moto.
Ibisobanuro by'icyarabu:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا لَقِيتُمُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ زَحۡفٗا فَلَا تُوَلُّوهُمُ ٱلۡأَدۡبَارَ
E inu amene mwakhulupirira! Pamene mukumana nawo (pa nkhondo) amene sadakhulupirire alikudza kwa inu mwa unyinji musawatembenuzire misana kuthawa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَمَن يُوَلِّهِمۡ يَوۡمَئِذٖ دُبُرَهُۥٓ إِلَّا مُتَحَرِّفٗا لِّقِتَالٍ أَوۡ مُتَحَيِّزًا إِلَىٰ فِئَةٖ فَقَدۡ بَآءَ بِغَضَبٖ مِّنَ ٱللَّهِ وَمَأۡوَىٰهُ جَهَنَّمُۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ
Ndipo amene adzawatembenuzire msana kuthawa pa tsikulo - osati kutembenuka (kwa ndale) kofuna kumenyana kapena kukalowa m’gulu (la Asilamu ena) - ndiye kuti adziitanira mkwiyo wochokera kwa Allah; ndipo malo ake ndi ku Jahannam, kumeneko ndi ku malo koipa kubwererapo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Isura: Al An’fal
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro bya Qur'an Ntagatifu mu rurimi rw'igi Chewa - Khaled Ibrahim Betala. - Ishakiro ry'ibisobanuro

Yasobanuwe na Khaled Ibrahim Betala.

Gufunga