Check out the new design

Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - Përkthimi çiçevë - Khalid Ibrahim Betiala * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: El Kehf   Ajeti:
فَلَمَّا جَاوَزَا قَالَ لِفَتَىٰهُ ءَاتِنَا غَدَآءَنَا لَقَدۡ لَقِينَا مِن سَفَرِنَا هَٰذَا نَصَبٗا
Pamene adapita patsogolo, adauza mnyamata wake, (kuti): “Tipatseni chakudya chathu chammawa; ndithu pa ulendo wathuwu takumana ndi zotopetsa.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ أَرَءَيۡتَ إِذۡ أَوَيۡنَآ إِلَى ٱلصَّخۡرَةِ فَإِنِّي نَسِيتُ ٱلۡحُوتَ وَمَآ أَنسَىٰنِيهُ إِلَّا ٱلشَّيۡطَٰنُ أَنۡ أَذۡكُرَهُۥۚ وَٱتَّخَذَ سَبِيلَهُۥ فِي ٱلۡبَحۡرِ عَجَبٗا
(Mnyamata) adati: “Kodi mwaona pamene tidapumula paja, pathanthwe ndipomwe ndidaiwala (kuti ndikuuzeni) za nsombayo ndipo palibe wandiiwalitsa koma satana basi, kuti ndisaikumbukire. Iyo idatenga njira yake kunka m’nyanja, mododometsa.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ ذَٰلِكَ مَا كُنَّا نَبۡغِۚ فَٱرۡتَدَّا عَلَىٰٓ ءَاثَارِهِمَا قَصَصٗا
(Mûsa) adati : “Pamenepo ndi pomwe timafuna.” Choncho adabwerera m’mbuyo potsatira njira yawo (yomweyo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَوَجَدَا عَبۡدٗا مِّنۡ عِبَادِنَآ ءَاتَيۡنَٰهُ رَحۡمَةٗ مِّنۡ عِندِنَا وَعَلَّمۡنَٰهُ مِن لَّدُنَّا عِلۡمٗا
Ndipo adampeza kapolo (Khidwiri) yemwe ndi m’modzi wa akapolo athu amene tidampatsa chifundo chochokera kwa Ife, (yemwenso) tidamphunzitsa maphunziro ambiri kuchokera kwa Ife.
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ لَهُۥ مُوسَىٰ هَلۡ أَتَّبِعُكَ عَلَىٰٓ أَن تُعَلِّمَنِ مِمَّا عُلِّمۡتَ رُشۡدٗا
Mûsa adati kwa iye: “Kodi ndingakutsate kuti undiphunzitse chiongoko chomwe waphunzitsidwa?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ إِنَّكَ لَن تَسۡتَطِيعَ مَعِيَ صَبۡرٗا
Adati: “Ndithu iwe siutha kupirira nane! (Uwona zomwe sungathe kupirira nazo).”
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَكَيۡفَ تَصۡبِرُ عَلَىٰ مَا لَمۡ تُحِطۡ بِهِۦ خُبۡرٗا
“Kodi ungapirire bwanji ndi zinthu zomwe sukuzidziwa chinsinsi chake?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ سَتَجِدُنِيٓ إِن شَآءَ ٱللَّهُ صَابِرٗا وَلَآ أَعۡصِي لَكَ أَمۡرٗا
(Mûsa) adati: “Ngati Allah afuna, undipeza ndili wopirira; ndipo sindinyoza lamulo lako.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ فَإِنِ ٱتَّبَعۡتَنِي فَلَا تَسۡـَٔلۡنِي عَن شَيۡءٍ حَتَّىٰٓ أُحۡدِثَ لَكَ مِنۡهُ ذِكۡرٗا
Adati: “Ngati unditsata usandifunse za chilichonse (chimene uchione) kufikira ine nditakuuza.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَٱنطَلَقَا حَتَّىٰٓ إِذَا رَكِبَا فِي ٱلسَّفِينَةِ خَرَقَهَاۖ قَالَ أَخَرَقۡتَهَا لِتُغۡرِقَ أَهۡلَهَا لَقَدۡ جِئۡتَ شَيۡـًٔا إِمۡرٗا
Choncho onse awiri adanyamuka kufikira pamene adakakwera m’chombo adachiboola. (Mûsa) adati: “Kodi wachiboola kuti uwamize ali m’menemo? Ndithu wachita chinthu chachikulu choipa.”[260]
[260] Tanthauzo lake nkuti pamene onse awiri adanyamuka adali kuyenda m’mphepete mwanyanja kufikira chombo chidawadutsa. Eni chombowo adamdziwa Khidhiru nawakweza onse awiri popanda malipiro. Atakwera m’chombomo Khidhiru adatenga nkhwangwa ndi kuzula thabwa limodzi la m’chombomo pomwe chombocho chidali pakatikati pa nyanja.
Musa ataona anati: “Bwanji ukuboola chombo pomwe anthuwa atinyamula mwaulere?” Ndipo adatenga kasanza nkuika pomwe panachotsedwa thabwapo.
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ أَلَمۡ أَقُلۡ إِنَّكَ لَن تَسۡتَطِيعَ مَعِيَ صَبۡرٗا
Adati: “Kodi sindidanene kuti iwe sutha kupirira nane?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالَ لَا تُؤَاخِذۡنِي بِمَا نَسِيتُ وَلَا تُرۡهِقۡنِي مِنۡ أَمۡرِي عُسۡرٗا
(Mûsa) adati: “Usandidzudzule chifukwa chakuiwala kwanga, ndipo usandipatse zovuta kwambiri pa khumbo langali (lofuna kukutsata).”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَٱنطَلَقَا حَتَّىٰٓ إِذَا لَقِيَا غُلَٰمٗا فَقَتَلَهُۥ قَالَ أَقَتَلۡتَ نَفۡسٗا زَكِيَّةَۢ بِغَيۡرِ نَفۡسٖ لَّقَدۡ جِئۡتَ شَيۡـٔٗا نُّكۡرٗا
Ndipo adanyamuka; mpaka pomwe adakumana ndi mnyamata wochepa, ndipo (mneneri Khidir) adamupha. Mûsa adati: “Ha! Wapha munthu wopanda cholakwa, pomwe sadaphe munthu mnzake? Ndithu wachita chinthu choipitsitsa.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: El Kehf
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - Përkthimi çiçevë - Khalid Ibrahim Betiala - Përmbajtja e përkthimeve

E përktheu Khalid Ibrahim Betala.

Mbyll