Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (165) Surja: Suretu El Enam
وَهُوَ ٱلَّذِي جَعَلَكُمۡ خَلَٰٓئِفَ ٱلۡأَرۡضِ وَرَفَعَ بَعۡضَكُمۡ فَوۡقَ بَعۡضٖ دَرَجَٰتٖ لِّيَبۡلُوَكُمۡ فِي مَآ ءَاتَىٰكُمۡۗ إِنَّ رَبَّكَ سَرِيعُ ٱلۡعِقَابِ وَإِنَّهُۥ لَغَفُورٞ رَّحِيمُۢ
Ndipo Iye ndi Yemwe wakuchitani kukhala am’lowam’malo pa dziko (kulowa m’malo mwa anzanu omwe adaonongeka). Ndipo wawatukula pa ulemelero (ndi pa chuma) ena a inu pamwamba pa ena kuti akuyeseni pa zomwe wakupatsani. (Amene apatsidwa chuma ndi ulemelero athandize amene sadapatsidwe. Ndipo amene sadapatsidwe apirire asalande chinthu chamwini). Ndithudi, Mbuye wako Ngwachangu pokhaulitsa. Ndiponso Iye Ngokhululuka kwabasi Ngwachisoni chosatha.[177]
[177] Ndime iyi ikusonyeza kuti kukhupuka ndi ulemelero, sindizo zizindikiro zosonyeza kuti munthuyo ngofunika kwa Allah. Ndiponso kusauka ndi kunyozeka sizizindikiro kuti munthuyo ngosafunika kwa Allah kapena wonyozeka kwa Allah. Koma kulemera, ulemelero, kusauka ndi kunyozeka.zonsezi amazipereka m’njira ya mayeso.
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (165) Surja: Suretu El Enam
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll