Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (150) Surja: Suretu El A’raf
وَلَمَّا رَجَعَ مُوسَىٰٓ إِلَىٰ قَوۡمِهِۦ غَضۡبَٰنَ أَسِفٗا قَالَ بِئۡسَمَا خَلَفۡتُمُونِي مِنۢ بَعۡدِيٓۖ أَعَجِلۡتُمۡ أَمۡرَ رَبِّكُمۡۖ وَأَلۡقَى ٱلۡأَلۡوَاحَ وَأَخَذَ بِرَأۡسِ أَخِيهِ يَجُرُّهُۥٓ إِلَيۡهِۚ قَالَ ٱبۡنَ أُمَّ إِنَّ ٱلۡقَوۡمَ ٱسۡتَضۡعَفُونِي وَكَادُواْ يَقۡتُلُونَنِي فَلَا تُشۡمِتۡ بِيَ ٱلۡأَعۡدَآءَ وَلَا تَجۡعَلۡنِي مَعَ ٱلۡقَوۡمِ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo pamene Mûsa adabwerera kwa anthu ake ali wokwiya, wodandaula (pomva zomwe zidachitikazo), adati: “Umlowam’malo wanu womwe mudandichitira pambuyo panga, ngoipa zedi. Kodi mudalifulumilira lamulo la Mbuye wanu; (mudachita zanuzanu musanadziwe chimene angakulamulireni Mulungu wanu)? Ndipo adawaponya pansi mapalewo (momwe mudalembedwa malamulo a chipembedzo chake). Nagwira mutu wa M’bale wake nkuukokera kwa iye. (kufuna kummenya chifukwa cha mkwiyo umene adali nawo. M’bale wakeyo) adati: “E iwe mwana wa mayi anga! Ndithu anthu (awa) adandiyesa wofooka, potero (sadamvere malangizo anga). Adatsala pang’ono kundipha. Choncho usawakondweretse adani (ndi chilango chako) pa ine, ndipo usandiike pamodzi ndi anthu oipa.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (150) Surja: Suretu El A’raf
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll