Check out the new design

அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அஸ்ஸாபாத்   வசனம்:
فَلَمَّآ أَسۡلَمَا وَتَلَّهُۥ لِلۡجَبِينِ
Pamene adagonjera onse awiri (chofuna cha Allah), ndipo (Ibrahim) adam’goneka chakumphumi (ndipo adatsimikiza kumupha).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَنَٰدَيۡنَٰهُ أَن يَٰٓإِبۡرَٰهِيمُ
Ndipo tidamuitana: “E iwe Ibrahim!”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَدۡ صَدَّقۡتَ ٱلرُّءۡيَآۚ إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
“Ndithu wavomereza maloto! (Choncho usamuphe mwana wakoyo).” Umo ndi momwe timawalipirira ochita zabwino.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ هَٰذَا لَهُوَ ٱلۡبَلَٰٓؤُاْ ٱلۡمُبِينُ
Ndithu amenewa ndimayeso oonekera.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَفَدَيۡنَٰهُ بِذِبۡحٍ عَظِيمٖ
Ndipo tidampulumutsa pompatsa nyama yayikulu (yoti apereke nsembe).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pake).
அரபு விரிவுரைகள்:
سَلَٰمٌ عَلَىٰٓ إِبۡرَٰهِيمَ
Mtendere ukhale pa Ibrahim!
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
M’menemo ndi mornwe timawalipirira ochita zabwino.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye adali mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَبَشَّرۡنَٰهُ بِإِسۡحَٰقَ نَبِيّٗا مِّنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Ndiponso tidamuuza nkhani yabwino (yoti akhala ndi mwana wotchedwa) Isihaqa; mneneri; wam’gulu la olungama.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَبَٰرَكۡنَا عَلَيۡهِ وَعَلَىٰٓ إِسۡحَٰقَۚ وَمِن ذُرِّيَّتِهِمَا مُحۡسِنٞ وَظَالِمٞ لِّنَفۡسِهِۦ مُبِينٞ
Ndipo tidamdalitsa iye ndi (mwana wake) Isihaqa; ndipo m’mbumba ya awiriwa mudapezeka abwino ndi odzichitira zoipa owonekera.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَقَدۡ مَنَنَّا عَلَىٰ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
Ndipo ndithu tidawachitira zabwino Mûsa ndi Haruna, (powapatsa uneneri ndi madalitso ambiri).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَنَجَّيۡنَٰهُمَا وَقَوۡمَهُمَا مِنَ ٱلۡكَرۡبِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidawapulumutsa (awiriwa) ndi anthu awo ku vuto lalikulu.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَنَصَرۡنَٰهُمۡ فَكَانُواْ هُمُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Ndipo tidawathangata (powagonjetsera adani awo), ndipo iwo adali opambana.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَءَاتَيۡنَٰهُمَا ٱلۡكِتَٰبَ ٱلۡمُسۡتَبِينَ
Ndipo tidawapatsa (Mûsa ndi Haruna) buku losonyeza poyera (malamulo).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَهَدَيۡنَٰهُمَا ٱلصِّرَٰطَ ٱلۡمُسۡتَقِيمَ
Ndipo tidawaongolera ku njira yolunjika.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِمَا فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndiponso tidawasiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pawo).
அரபு விரிவுரைகள்:
سَلَٰمٌ عَلَىٰ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
Mtendere ukhale pa Mûsa ndi Haruna!
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umu ndi momwe Ife timawalipirira ochita zabwino.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّهُمَا مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu awiriwa adali m’gulu la akapoio Athu okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ إِلۡيَاسَ لَمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo ndithu Iliyasa ndi mmodzi wa atumiki.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لِقَوۡمِهِۦٓ أَلَا تَتَّقُونَ
(Kumbuka) pamene adanena kwa anthu ake: “Bwanji simuopa (Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَتَدۡعُونَ بَعۡلٗا وَتَذَرُونَ أَحۡسَنَ ٱلۡخَٰلِقِينَ
“Mukupembedza (fano lotchedwa) Ba’la ndi kusiya (kupembedza) Wabwino zedi mwa olenga onse.”
அரபு விரிவுரைகள்:
ٱللَّهَ رَبَّكُمۡ وَرَبَّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Allah, Mbuye wanu ndi Mbuye wa makolo anu akale?”
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அஸ்ஸாபாத்
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

மொழிபெயர்த்தது காலித் இப்ராஹீம் பைதாலா.

மூடுக