Check out the new design

పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - చిచియో అనువాదం - ఖాలిద్ ఇబ్రాహీమ్ బైతాలా * - అనువాదాల విషయసూచిక


భావార్ధాల అనువాదం సూరహ్: అత్-తౌబహ్   వచనం:
وَٱلَّذِينَ ٱتَّخَذُواْ مَسۡجِدٗا ضِرَارٗا وَكُفۡرٗا وَتَفۡرِيقَۢا بَيۡنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَإِرۡصَادٗا لِّمَنۡ حَارَبَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ مِن قَبۡلُۚ وَلَيَحۡلِفُنَّ إِنۡ أَرَدۡنَآ إِلَّا ٱلۡحُسۡنَىٰۖ وَٱللَّهُ يَشۡهَدُ إِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
Ndipo (alipo achiphamaso ena) amene adamanga msikiti ndi cholinga chodzetsa masautso ndi (kulimbikitsa) kusakhulupirira Allah ndi kuwagawa okhulupirira (mu umodzi wawo) ndi kuupanga kukhala msasa wa omwe adamthira nkhondo Allah ndi Mtumiki Wake kale. Ndithu alumbira (ndikunena): “Sitidali ncholinga china (pomanga msikitiwo) koma ubwino.” Koma Allah akuikira umboni kuti iwo ngabodza.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
لَا تَقُمۡ فِيهِ أَبَدٗاۚ لَّمَسۡجِدٌ أُسِّسَ عَلَى ٱلتَّقۡوَىٰ مِنۡ أَوَّلِ يَوۡمٍ أَحَقُّ أَن تَقُومَ فِيهِۚ فِيهِ رِجَالٞ يُحِبُّونَ أَن يَتَطَهَّرُواْۚ وَٱللَّهُ يُحِبُّ ٱلۡمُطَّهِّرِينَ
Usaimilire (ndi kupemphera) m’menemo mpang’ono pomwe. Ndithu msikiti umene udakhazikitsidwa poyamba ncholinga choopa Allah ndiwo wofunika kuti uimilire m’menemo (ndi kupemphera). M’menemo muli anthu okonda kudziyeretsa (matupi ndi mitima yawo); ndipo Allah amakonda odziyeretsa.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
أَفَمَنۡ أَسَّسَ بُنۡيَٰنَهُۥ عَلَىٰ تَقۡوَىٰ مِنَ ٱللَّهِ وَرِضۡوَٰنٍ خَيۡرٌ أَم مَّنۡ أَسَّسَ بُنۡيَٰنَهُۥ عَلَىٰ شَفَا جُرُفٍ هَارٖ فَٱنۡهَارَ بِهِۦ فِي نَارِ جَهَنَّمَۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi amene wakhazikitsa maziko a chomanga chake chifukwa choopa Allah ndi kufunafuna chiyanjo (Chake), sindiye wabwino, kapena Yemwe wakhazikitsa maziko a chomanga chake m’mphepete mwa dzenje (lakuya) lomwe dothi lake likugumukira (m’dzenjemo) ndipo nkugwa pamodzi naye m’moto wa Jahannam, (ameneyu ndiye wabwino)? Ndithudi, Allah saongolera anthu ochita zoipa.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
لَا يَزَالُ بُنۡيَٰنُهُمُ ٱلَّذِي بَنَوۡاْ رِيبَةٗ فِي قُلُوبِهِمۡ إِلَّآ أَن تَقَطَّعَ قُلُوبُهُمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٌ
Chomanga chawo chomwe adachimanga sichileka kudzetsa chikaiko ndi kusakhazikika m’mitima mwawo kufikira mitima yawo itaduka (ndi madandaulo kapena imfa). Ndipo Allah Ngodziwa (chilichonse), Ngwanzeru zakuya (m’zochitachita Zake).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
۞ إِنَّ ٱللَّهَ ٱشۡتَرَىٰ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ أَنفُسَهُمۡ وَأَمۡوَٰلَهُم بِأَنَّ لَهُمُ ٱلۡجَنَّةَۚ يُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَيَقۡتُلُونَ وَيُقۡتَلُونَۖ وَعۡدًا عَلَيۡهِ حَقّٗا فِي ٱلتَّوۡرَىٰةِ وَٱلۡإِنجِيلِ وَٱلۡقُرۡءَانِۚ وَمَنۡ أَوۡفَىٰ بِعَهۡدِهِۦ مِنَ ٱللَّهِۚ فَٱسۡتَبۡشِرُواْ بِبَيۡعِكُمُ ٱلَّذِي بَايَعۡتُم بِهِۦۚ وَذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Ndithu Allah wagula kwa okhulupirira moyo wawo ndi chuma chawo (kuti apereke moyo wawo ndi chuma chawo pomenya nkhondo pa njira ya Allah) kuti iwo alandire Munda wamtendere. Akumenya nkhondo pa njira ya Allah, ndipo akupha ndi kuphedwa. Ili ndi lonjezo loona lokakamizika pa Iye lomwe likupezeka m’buku la Taurati, Injili ndi Qur’an. Kodi ndani wokwaniritsa lonjezo lake kuposa Allah? Choncho kondwerani ndi kugulitsa kwanu komwe mwagulitsana Naye. Kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
 
భావార్ధాల అనువాదం సూరహ్: అత్-తౌబహ్
సూరాల విషయసూచిక పేజీ నెంబరు
 
పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - చిచియో అనువాదం - ఖాలిద్ ఇబ్రాహీమ్ బైతాలా - అనువాదాల విషయసూచిక

దానిని అనువదించినది ఖాలిద్ ఇబ్రాహీం పీటాలా.

మూసివేయటం