Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Ayet: (19) Sure: Sûratu Yûnus
وَمَا كَانَ ٱلنَّاسُ إِلَّآ أُمَّةٗ وَٰحِدَةٗ فَٱخۡتَلَفُواْۚ وَلَوۡلَا كَلِمَةٞ سَبَقَتۡ مِن رَّبِّكَ لَقُضِيَ بَيۡنَهُمۡ فِيمَا فِيهِ يَخۡتَلِفُونَ
Ndipo ndithudi anthu kalero (m’nthawi ya Adam) adali mpingo umodzi (opembedza Allah), koma adasiyana (pambuyo pake). Ndipo pakadapanda liwu lochokera kwa Mbuye wako, lomwe lidatsogola (lakuti adzawalanga tsiku la Qiyâma), ndithu kukadaweruzidwa pakati pawo m’zomwe adali kusiyana.[218]
[218] Ndithudi, anthu mchilengedwe chawo adali a mpingo umodzi wogonjera Allah mwa chilengedwe. Kenako Allah adawatumizira aneneri kuti awatsogolere kunjira Yake molingana ndi chilamulo chake Allah. Koma ngakhale zili tere anthu adali ndi ufulu mwa chilengedwe chawo kulandira choipa kapena chabwino. Potero, choipa chidawagonjetsa ena a iwo natsata zilakolako za satana. Nasiyana ndi anzawo chifukwa chazimenezo. Komatu padali lamulo la Allah la pachiyambi loti oipa sadzawalanga mwachangu koma kufikira nthawi yawo itakwana. Pakadapanda lamuloli ndiye kuti onse akadawalanga nthawi yomweyo.
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Ayet: (19) Sure: Sûratu Yûnus
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا - Mealler fihristi

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Kapat