クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (19) 章: ユーヌス章
وَمَا كَانَ ٱلنَّاسُ إِلَّآ أُمَّةٗ وَٰحِدَةٗ فَٱخۡتَلَفُواْۚ وَلَوۡلَا كَلِمَةٞ سَبَقَتۡ مِن رَّبِّكَ لَقُضِيَ بَيۡنَهُمۡ فِيمَا فِيهِ يَخۡتَلِفُونَ
Ndipo ndithudi anthu kalero (m’nthawi ya Adam) adali mpingo umodzi (opembedza Allah), koma adasiyana (pambuyo pake). Ndipo pakadapanda liwu lochokera kwa Mbuye wako, lomwe lidatsogola (lakuti adzawalanga tsiku la Qiyâma), ndithu kukadaweruzidwa pakati pawo m’zomwe adali kusiyana.[218]
[218] Ndithudi, anthu mchilengedwe chawo adali a mpingo umodzi wogonjera Allah mwa chilengedwe. Kenako Allah adawatumizira aneneri kuti awatsogolere kunjira Yake molingana ndi chilamulo chake Allah. Koma ngakhale zili tere anthu adali ndi ufulu mwa chilengedwe chawo kulandira choipa kapena chabwino. Potero, choipa chidawagonjetsa ena a iwo natsata zilakolako za satana. Nasiyana ndi anzawo chifukwa chazimenezo. Komatu padali lamulo la Allah la pachiyambi loti oipa sadzawalanga mwachangu koma kufikira nthawi yawo itakwana. Pakadapanda lamuloli ndiye kuti onse akadawalanga nthawi yomweyo.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (19) 章: ユーヌス章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる