Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Ayet: (1) Sure: Sûratu'l-Mâide

Sûratu'l-Mâide

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَوۡفُواْ بِٱلۡعُقُودِۚ أُحِلَّتۡ لَكُم بَهِيمَةُ ٱلۡأَنۡعَٰمِ إِلَّا مَا يُتۡلَىٰ عَلَيۡكُمۡ غَيۡرَ مُحِلِّي ٱلصَّيۡدِ وَأَنتُمۡ حُرُمٌۗ إِنَّ ٱللَّهَ يَحۡكُمُ مَا يُرِيدُ
E inu amene mwakhulupirira! Kwaniritsani mapangano onse (omwe ali pakati panu ndi anthu anzanu). Kwalolezedwa kwa inu (kudya nyama ya) ziweto (monga ngamira, ng’ombe ndi mbuzi), kupatula chomwe mukuuzidwa (kuti ncholetsedwa). Koma nkosaloledwa kwa inu kuchita ulenje mutalowa m’mapemphero a Hajj, (kapena muli m’nthaka yopatulika ya ku Makka). Ndithudi, Allah akulamula chimene wafuna.[155]
[155] Chisilamu chimalemekeza zinthu zogwilira ntchito ya chipembedzo, monga ziweto zimene amazitumiza ku Makka ncholinga choti akazizinge kumeneko monga sadaka yopereka konko. Ndipo anthu okachita mapemphero a Hajjiwo, ziweto amaziveka zizindikiro zosonyeza kuti nziweto zomwe akukazipereka monga nsembe kwa Allah. Ndipo nyamazo zimakhala zopatulika. Choncho sibwino kuswa kupatulika kumeneku pozilanda mwachifwamba ndi kuzipha zisanafike pamalo pake poziphera.
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Ayet: (1) Sure: Sûratu'l-Mâide
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا - Mealler fihristi

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Kapat