قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ آیت: (1) سورت: سورۂ مائدہ

سورۂ مائدہ

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَوۡفُواْ بِٱلۡعُقُودِۚ أُحِلَّتۡ لَكُم بَهِيمَةُ ٱلۡأَنۡعَٰمِ إِلَّا مَا يُتۡلَىٰ عَلَيۡكُمۡ غَيۡرَ مُحِلِّي ٱلصَّيۡدِ وَأَنتُمۡ حُرُمٌۗ إِنَّ ٱللَّهَ يَحۡكُمُ مَا يُرِيدُ
E inu amene mwakhulupirira! Kwaniritsani mapangano onse (omwe ali pakati panu ndi anthu anzanu). Kwalolezedwa kwa inu (kudya nyama ya) ziweto (monga ngamira, ng’ombe ndi mbuzi), kupatula chomwe mukuuzidwa (kuti ncholetsedwa). Koma nkosaloledwa kwa inu kuchita ulenje mutalowa m’mapemphero a Hajj, (kapena muli m’nthaka yopatulika ya ku Makka). Ndithudi, Allah akulamula chimene wafuna.[155]
[155] Chisilamu chimalemekeza zinthu zogwilira ntchito ya chipembedzo, monga ziweto zimene amazitumiza ku Makka ncholinga choti akazizinge kumeneko monga sadaka yopereka konko. Ndipo anthu okachita mapemphero a Hajjiwo, ziweto amaziveka zizindikiro zosonyeza kuti nziweto zomwe akukazipereka monga nsembe kwa Allah. Ndipo nyamazo zimakhala zopatulika. Choncho sibwino kuswa kupatulika kumeneku pozilanda mwachifwamba ndi kuzipha zisanafike pamalo pake poziphera.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ آیت: (1) سورت: سورۂ مائدہ
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ - ترجمے کی لسٹ

قرآن کریم کے معانی کا شیشیوا ترجمہ، ترجمہ خالد ابراہیم بيتلا نے کیا ہے۔نسخہ ۲۰۲۰م۔

بند کریں