قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (100) سۈرە: سۈرە نىسا
۞ وَمَن يُهَاجِرۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ يَجِدۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُرَٰغَمٗا كَثِيرٗا وَسَعَةٗۚ وَمَن يَخۡرُجۡ مِنۢ بَيۡتِهِۦ مُهَاجِرًا إِلَى ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ ثُمَّ يُدۡرِكۡهُ ٱلۡمَوۡتُ فَقَدۡ وَقَعَ أَجۡرُهُۥ عَلَى ٱللَّهِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Ndipo amene angasamuke pa njira ya Allah (chifukwa cha chipembedzo chake,) apeza malo ambiri m’dzikomo othawira ndikupeza bwino. Ndipo amene angatuluke m’nyumba mwake kuti asamuke chifukwa cha Allah ndi Mtumiki Wake, kenako nkumpeza imfa (m’njira), ndithu malipiro ake atsimikizika kwa Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.[137]
[137] Apa akuwalimbikitsa za kusamuka ndi kuwauza kuti kumene akupitako akapeza bwino. Akuwalimbikitsanso okalamba ndi odwala kuti asamuke. Ngati atafera pa njira kuwerengedwa kuti adasamukabe ndipo adzapeza mphoto yonga ya yemwe adasamuka nkukakhala ku Madina pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) ndi kukathandiza kukamenya nkhondo yoteteza Chisilamu kwa adani. Ndichimodzomodzi munthu akapita ku Makka kukachita Hajj ndipo nkumwalira Hajjiyo asanachite, kapena asanamalize zina zofunika pa Hajj, kwa Allah amamuwerenga kuti wachita mapemphero a Hajj. Komabe abale ake akhoza kukamchitiranso mapemphero a Hajj.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (100) سۈرە: سۈرە نىسا
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش