Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Verset: (100) Sourate: AN-NISÂ’
۞ وَمَن يُهَاجِرۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ يَجِدۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُرَٰغَمٗا كَثِيرٗا وَسَعَةٗۚ وَمَن يَخۡرُجۡ مِنۢ بَيۡتِهِۦ مُهَاجِرًا إِلَى ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ ثُمَّ يُدۡرِكۡهُ ٱلۡمَوۡتُ فَقَدۡ وَقَعَ أَجۡرُهُۥ عَلَى ٱللَّهِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Ndipo amene angasamuke pa njira ya Allah (chifukwa cha chipembedzo chake,) apeza malo ambiri m’dzikomo othawira ndikupeza bwino. Ndipo amene angatuluke m’nyumba mwake kuti asamuke chifukwa cha Allah ndi Mtumiki Wake, kenako nkumpeza imfa (m’njira), ndithu malipiro ake atsimikizika kwa Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.[137]
[137] Apa akuwalimbikitsa za kusamuka ndi kuwauza kuti kumene akupitako akapeza bwino. Akuwalimbikitsanso okalamba ndi odwala kuti asamuke. Ngati atafera pa njira kuwerengedwa kuti adasamukabe ndipo adzapeza mphoto yonga ya yemwe adasamuka nkukakhala ku Madina pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) ndi kukathandiza kukamenya nkhondo yoteteza Chisilamu kwa adani. Ndichimodzomodzi munthu akapita ku Makka kukachita Hajj ndipo nkumwalira Hajjiyo asanachite, kapena asanamalize zina zofunika pa Hajj, kwa Allah amamuwerenga kuti wachita mapemphero a Hajj. Komabe abale ake akhoza kukamchitiranso mapemphero a Hajj.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Verset: (100) Sourate: AN-NISÂ’
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture