قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا * - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى


مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (119) سۈرە: سۈرە نىسا
وَلَأُضِلَّنَّهُمۡ وَلَأُمَنِّيَنَّهُمۡ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُبَتِّكُنَّ ءَاذَانَ ٱلۡأَنۡعَٰمِ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُغَيِّرُنَّ خَلۡقَ ٱللَّهِۚ وَمَن يَتَّخِذِ ٱلشَّيۡطَٰنَ وَلِيّٗا مِّن دُونِ ٱللَّهِ فَقَدۡ خَسِرَ خُسۡرَانٗا مُّبِينٗا
“Ndipo ndikawasokeretsa ndi kuwapatsa ziyembekezo (zabodza) ndithu ndikawalamula kuti azikadula makutu a ziweto, ndipo ndikawalamulanso kuti azikasintha chilengedwe cha Allah.” Ndipo amene angamulole satana kukhala mtetezi wake kusiya Allah, ndiye kuti wataika koonekera.[149]
[149] (1) Kukhala ndi chiyembekezo choti Allah adzawakhululukira pakuti iye ngokhululuka, Ngwachifundo. (2) Kuti ukachita zakutizakuti kapena ukawerenga duwa yakutiyakuti machimo ako onse adzakufafanizira ngakhale kuti udakwatula zinthu za anthu. (3) Kuti wolemekezeka uje adzatiwombola ngati tilumikizana naye. (4) Kuti mneneri wakutiwakuti adzaitana omtsatira ake kuti akalowe ku Munda wa mtendere. (5) Kuti Mtumiki sadzakhala wokondwa kuona anthu ake akuponyedwa ku Moto. (6) Kukhala ndi chiyembekezo choti ngati munthu ndiwe Msilamu basi sukalowa ku Jahannam. Ndipo satanayu amanyenganso Akhrisitu kuti ngati akhulupilira Isa (Yesu) basi sakalowa ku Moto. Ndipo Ayuda amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati akhulupilira m’chipembedzo cha chiyuda sakalowa ku Moto. Nawonso opembedza moto ndi Abudha amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati atsata chibudha basi apulumuka.
ئەرەپچە تەپسىرلەر:
 
مەنالار تەرجىمىسى ئايەت: (119) سۈرە: سۈرە نىسا
سۈرە مۇندەرىجىسى بەت نومۇرى
 
قۇرئان كەرىم مەنىلىرىنىڭ تەرجىمىسى - الترجمة الشيشيوا - تەرجىمىلەر مۇندەرىجىسى

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

تاقاش