Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Câu: (119) Chương: Chương Al-Nisa'
وَلَأُضِلَّنَّهُمۡ وَلَأُمَنِّيَنَّهُمۡ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُبَتِّكُنَّ ءَاذَانَ ٱلۡأَنۡعَٰمِ وَلَأٓمُرَنَّهُمۡ فَلَيُغَيِّرُنَّ خَلۡقَ ٱللَّهِۚ وَمَن يَتَّخِذِ ٱلشَّيۡطَٰنَ وَلِيّٗا مِّن دُونِ ٱللَّهِ فَقَدۡ خَسِرَ خُسۡرَانٗا مُّبِينٗا
“Ndipo ndikawasokeretsa ndi kuwapatsa ziyembekezo (zabodza) ndithu ndikawalamula kuti azikadula makutu a ziweto, ndipo ndikawalamulanso kuti azikasintha chilengedwe cha Allah.” Ndipo amene angamulole satana kukhala mtetezi wake kusiya Allah, ndiye kuti wataika koonekera.[149]
[149] (1) Kukhala ndi chiyembekezo choti Allah adzawakhululukira pakuti iye ngokhululuka, Ngwachifundo. (2) Kuti ukachita zakutizakuti kapena ukawerenga duwa yakutiyakuti machimo ako onse adzakufafanizira ngakhale kuti udakwatula zinthu za anthu. (3) Kuti wolemekezeka uje adzatiwombola ngati tilumikizana naye. (4) Kuti mneneri wakutiwakuti adzaitana omtsatira ake kuti akalowe ku Munda wa mtendere. (5) Kuti Mtumiki sadzakhala wokondwa kuona anthu ake akuponyedwa ku Moto. (6) Kukhala ndi chiyembekezo choti ngati munthu ndiwe Msilamu basi sukalowa ku Jahannam. Ndipo satanayu amanyenganso Akhrisitu kuti ngati akhulupilira Isa (Yesu) basi sakalowa ku Moto. Ndipo Ayuda amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati akhulupilira m’chipembedzo cha chiyuda sakalowa ku Moto. Nawonso opembedza moto ndi Abudha amawauzanso chimodzimodzi kuti ngati atsata chibudha basi apulumuka.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Câu: (119) Chương: Chương Al-Nisa'
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại