Check out the new design

قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ سورت: یوسف   آیت:
۞ وَمَآ أُبَرِّئُ نَفۡسِيٓۚ إِنَّ ٱلنَّفۡسَ لَأَمَّارَةُۢ بِٱلسُّوٓءِ إِلَّا مَا رَحِمَ رَبِّيٓۚ إِنَّ رَبِّي غَفُورٞ رَّحِيمٞ
۞ “Ndipo ine sindikuyeretsa mtima wanga. Ndithu mtima uliwonse umalamulira kwambiri ku zoipa kupatula umene Mbuye wanga wauchitira chifundo. Ndithudi, Mbuye wanga Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.”
عربی تفاسیر:
وَقَالَ ٱلۡمَلِكُ ٱئۡتُونِي بِهِۦٓ أَسۡتَخۡلِصۡهُ لِنَفۡسِيۖ فَلَمَّا كَلَّمَهُۥ قَالَ إِنَّكَ ٱلۡيَوۡمَ لَدَيۡنَا مَكِينٌ أَمِينٞ
Choncho Mfumu idati: “Mubwere naye kwa ine kuti ine mwini ndimsankhe.” Ndipo pamene adayankhula naye, (Mfumu) idati: “Ndithu iwe lero kwa ife wakhala wolemekezeka, wokhulupirika.”
عربی تفاسیر:
قَالَ ٱجۡعَلۡنِي عَلَىٰ خَزَآئِنِ ٱلۡأَرۡضِۖ إِنِّي حَفِيظٌ عَلِيمٞ
(Yûsuf) adati: “Ndiikeni kukhala muyang’aniri wa nkhokwe za dzinthu zam’dziko lonse. Ndithudi, ine ndine msungi wodziwa.”
عربی تفاسیر:
وَكَذَٰلِكَ مَكَّنَّا لِيُوسُفَ فِي ٱلۡأَرۡضِ يَتَبَوَّأُ مِنۡهَا حَيۡثُ يَشَآءُۚ نُصِيبُ بِرَحۡمَتِنَا مَن نَّشَآءُۖ وَلَا نُضِيعُ أَجۡرَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo motero tidampatsa ulemelero Yûsuf m’dziko (la Iguputo); amakhala m’menemo paliponse pamene wafuna. Timam’bweretsera chifundo Chathu amene tamfuna, ndipo sitisokoneza malipiro a ochita zabwino.
عربی تفاسیر:
وَلَأَجۡرُ ٱلۡأٓخِرَةِ خَيۡرٞ لِّلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَكَانُواْ يَتَّقُونَ
Ndithudi malipiro a tsiku la chimaliziro ngabwino zedi kwa amene akhulupirira ndipo adali kumuopa (Allah).
عربی تفاسیر:
وَجَآءَ إِخۡوَةُ يُوسُفَ فَدَخَلُواْ عَلَيۡهِ فَعَرَفَهُمۡ وَهُمۡ لَهُۥ مُنكِرُونَ
Ndipo adadza abale (ake) a Yûsuf (kukafuna chakudya kumeneko pamene ku Kenani kudagwa chilala chadzaoneni) ndikulowa kwa iye, ndipo (iye) adawazindikira pomwe iwo sankamzindikira.
عربی تفاسیر:
وَلَمَّا جَهَّزَهُم بِجَهَازِهِمۡ قَالَ ٱئۡتُونِي بِأَخٖ لَّكُم مِّنۡ أَبِيكُمۡۚ أَلَا تَرَوۡنَ أَنِّيٓ أُوفِي ٱلۡكَيۡلَ وَأَنَا۠ خَيۡرُ ٱلۡمُنزِلِينَ
Ndipo pamene adawakonzera chakudya chawo, adati: “(Ngatimudzabwereranso kachiwiri) mudzabwere ndi m‘bale wanu wa kumbali ya bambo anu, kodi simuona kuti ine ndikukwaniritsa muyeso, ndipo ndine wabwino kwambiri polandira (alendo)?”
عربی تفاسیر:
فَإِن لَّمۡ تَأۡتُونِي بِهِۦ فَلَا كَيۡلَ لَكُمۡ عِندِي وَلَا تَقۡرَبُونِ
“Koma ngati simudzandibweretsera iye, simudzakhala ndi mulingo (wachakudya) kwa ine, ndipo musadzandiyandikire.”
عربی تفاسیر:
قَالُواْ سَنُرَٰوِدُ عَنۡهُ أَبَاهُ وَإِنَّا لَفَٰعِلُونَ
(Iwo) adati: “Tikayesetsa kuwanyengelera bambo wake za iye (kufikira akatipatse). Ndithu ife tikachita zimenezi.”
عربی تفاسیر:
وَقَالَ لِفِتۡيَٰنِهِ ٱجۡعَلُواْ بِضَٰعَتَهُمۡ فِي رِحَالِهِمۡ لَعَلَّهُمۡ يَعۡرِفُونَهَآ إِذَا ٱنقَلَبُوٓاْ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِمۡ لَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
Ndipo (Yûsuf) adati kwa anyamata ake a ntchito: “Ikani chuma chawo m’mitolo yawo kuti akachizindikire akabwerera ku mawanja awo. (Tachita izi kuti) mwina angabwelerenso (kuno).”
عربی تفاسیر:
فَلَمَّا رَجَعُوٓاْ إِلَىٰٓ أَبِيهِمۡ قَالُواْ يَٰٓأَبَانَا مُنِعَ مِنَّا ٱلۡكَيۡلُ فَأَرۡسِلۡ مَعَنَآ أَخَانَا نَكۡتَلۡ وَإِنَّا لَهُۥ لَحَٰفِظُونَ
Ndipo pamene adabwerera kwa bambo wawo, adati: “E bambo wathu! Tikamanidwa muyeso wa chakudya (pa ulendo wachiwiri pokhapokha titsagane ndi m’bale wathuyu). Choncho mtumizeni m’bale wathu pamodzi ndi ife kuti akatipimire (mlingo wokwana); ndithu ife tikamsunga.”
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ سورت: یوسف
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا - ترجمے کی لسٹ

خالد ابراہیم پیٹالا نے ترجمہ کیا۔

بند کریں