قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ آیت: (41) سورت: سورۂ عنکبوت
مَثَلُ ٱلَّذِينَ ٱتَّخَذُواْ مِن دُونِ ٱللَّهِ أَوۡلِيَآءَ كَمَثَلِ ٱلۡعَنكَبُوتِ ٱتَّخَذَتۡ بَيۡتٗاۖ وَإِنَّ أَوۡهَنَ ٱلۡبُيُوتِ لَبَيۡتُ ٱلۡعَنكَبُوتِۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Fanizo la amene adzipangira milungu yabodza kusiya Allah, lili ngati fanizo la kangaude (yemwe) wadzipangira nyumba (kuti imsunge, pomwe nyumbayo siingathe kumsunga m’nyengo yozizira kapena yotentha), ndithu nyumba yomwe ili yofooka kwambiri ndi nyumba ya kangaude, akadakhala akudziwa.[304]
[304] M’ndime iyi Allah akufanizira munthu wopembedza mafano ndicholinga choti mafanowo adzimthangata pomudzetsera zabwino ndi kumchotsera zoipa, kuti ali ngati kangaude yemwe wamanga nyumba ndi cholinga choti imteteze ku chisanu ndi kutentha pomwe nyumbayo njofooka yomwe siingathe kumteteza ku chisanu kapena kudzuwa. Izi zili chimodzimodzi ndi wopembedza mafano. Mafanowo sangamudzetsere zabwino kapena kumchotsera zoipa.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ آیت: (41) سورت: سورۂ عنکبوت
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ - ترجمے کی لسٹ

قرآن کریم کے معانی کا شیشیوا ترجمہ، ترجمہ خالد ابراہیم بيتلا نے کیا ہے۔نسخہ ۲۰۲۰م۔

بند کریں