قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ آیت: (13) سورت: سورۂ مائدہ
فَبِمَا نَقۡضِهِم مِّيثَٰقَهُمۡ لَعَنَّٰهُمۡ وَجَعَلۡنَا قُلُوبَهُمۡ قَٰسِيَةٗۖ يُحَرِّفُونَ ٱلۡكَلِمَ عَن مَّوَاضِعِهِۦ وَنَسُواْ حَظّٗا مِّمَّا ذُكِّرُواْ بِهِۦۚ وَلَا تَزَالُ تَطَّلِعُ عَلَىٰ خَآئِنَةٖ مِّنۡهُمۡ إِلَّا قَلِيلٗا مِّنۡهُمۡۖ فَٱعۡفُ عَنۡهُمۡ وَٱصۡفَحۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Choncho chifukwa chakuswa pangano lawo, tidawatembelera; ndipo tidaumitsa mitima yawo. Ankasintha mawu (a Allah omwe adali m’mabuku a Taurat ndi Injili) kuwachotsa m’malo mwake ndipo adasiya kukwaniritsa gawo lalikulu la zomwe adakumbutsidwa. Ndipo ukhala ukuona (iwe Mtumiki {s.a.w}) chinyengo mwa ambiri a iwo, kupatula ochepa a iwo. Choncho akhululukire ndi kuwaleka. Ndithudi, Allah amakonda ochita zabwino.[159]
[159] Ndime iyi ikupitirizanso kutchula zina mwa zoipa za Ayuda. Ndipo zina mwa izozi ndiko kusintha mawu a m’buku lawo lomwe Allah adawavumbulutsira. Iwo ankachotsamo mawu omwe sadali kuwafuna naikamo amene ankawafuna. Zoterezi Akhrisitu anazichitanso. Ndipo akuchitabe mpaka lero. Mabaibulo awo omwe akusindikiza nkuwagawa m’maiko athu kuno ku Africa ndi kwina kulikonse ngati utaona mofatsa omwe asindikiza posachedwapa upeza kusiyana pang’ono ndi omwe adasindikiza m’mbuyomu. (a) Mwina akuchotsa zimene zidalimo (b) Kapena akuikamo zomwe mudalibe (c) Mwina matanthauzo achiganizo amawasinthiratu kusiyana ndi momwe zidalili m’buku lomwe adasindikiza kale. Zonsezi zikusonyeza kuti amenewa ndiwo machitidwe awo pofuna kukopa anthu ambiri kuchipembedzo chawo. Akaona kuti ichi chikopa anthu ambiri, amachiikamo nanena kuti ndi mawu a Mulungu. Ndipo akaona kuti malamulo awa apirikitsa anthu amawachotsa kapena kuwachepetsa mphamvu yake. Umo ndimomwe alili machitidwe awo.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ آیت: (13) سورت: سورۂ مائدہ
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ - ترجمے کی لسٹ

قرآن کریم کے معانی کا شیشیوا ترجمہ، ترجمہ خالد ابراہیم بيتلا نے کیا ہے۔نسخہ ۲۰۲۰م۔

بند کریں