Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Оят: (69) Сура: Тоҳа сураси
وَأَلۡقِ مَا فِي يَمِينِكَ تَلۡقَفۡ مَا صَنَعُوٓاْۖ إِنَّمَا صَنَعُواْ كَيۡدُ سَٰحِرٖۖ وَلَا يُفۡلِحُ ٱلسَّاحِرُ حَيۡثُ أَتَىٰ
“Ndipo ponya chimene chili kudzanja lako ladzanjadzanja (ndodo); chimeza zomwe apanga; ndithu iwo apanga matsenga a mfiti ndipo mfiti siingapambane paliponse pamene yadza.”[281]
[281] Ibun Kathir adati: Pamene Musa adaponya ndodo idasanduka chinjoka chachikulu chokhala ndi miyendo ndi khosi ndi mutu ndi mano. Chidayamba kutsatira zingwezo ndi ndodozo mpaka chidameza zonsezo uku anthu akuona masomphenya masana. Amatsenga ataona zimenezo, adazindikira mwachitsimikizo kuti kusanduka kwa ndodoyo kukhala chinjoka sikudali kwaufiti kapena matsenga. Koma chidali choonadi chopanda chipeneko. Ndipo pamenepo onse adagwa ndi kulambira Allah. Tero chizizwa cha Allah chidatsimikizika. Koma zopanda pake zidapita pachabe.
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Оят: (69) Сура: Тоҳа сураси
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Қуръон Карим маъноларининг чевача таржимаси, мутаржим: Холид Иброҳим Бетала, 2020 йилда нашр қилинган

Ёпиш