የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (19) ምዕራፍ: ሱረቱ አን-ኒሳዕ
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا يَحِلُّ لَكُمۡ أَن تَرِثُواْ ٱلنِّسَآءَ كَرۡهٗاۖ وَلَا تَعۡضُلُوهُنَّ لِتَذۡهَبُواْ بِبَعۡضِ مَآ ءَاتَيۡتُمُوهُنَّ إِلَّآ أَن يَأۡتِينَ بِفَٰحِشَةٖ مُّبَيِّنَةٖۚ وَعَاشِرُوهُنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ فَإِن كَرِهۡتُمُوهُنَّ فَعَسَىٰٓ أَن تَكۡرَهُواْ شَيۡـٔٗا وَيَجۡعَلَ ٱللَّهُ فِيهِ خَيۡرٗا كَثِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Sikovomerezedwa kwa inu kuwalowa chokolo akazi mowakakamiza. Ndipo musawaletse (kukwatiwa ndi amuna ena) ndi cholinga choti muwalande zina mwa zomwe mudawapatsa, (nkosaloledwa kutero) kupatula ngati atachita choipa choonekera. Ndipo khalani nawo mwa ubwino. Ngati mutawada (musalekane nawo), mwina mungade chinthu chomwe Allah waika zabwino zambiri mkati mwake.[116]
[116] Nthawi ya umbuli, chikhalidwe cha Arabu chidali chonchi:- Tate wa munthu akamwalira ana ake amamlowera chokolo akazi ake omwe sadabereke anawo. Mwana aliyense amalowa chokolo mwa mkazi watate wake yemwe sadali mayi wake wom’bala.
a) Akafuna kumkwatira adali kumtenga.
b) Ndipo akafuna kumkwatitsa kwa mwamuna wina, amamlamula ndalama mwamunayo iye natenga ndalamazo.
c) Kapena amangomuvutitsavutitsa kuti akafuna adziombole yekha pomlipira ndalama mwanayo.
d) Kapena amangommanga kuti asakwatiwenso mpaka imfa yake. Choncho apa Allah akuletsa machitidwe oipawa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (19) ምዕራፍ: ሱረቱ አን-ኒሳዕ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት