Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Versículo: (19) Surah: Suratu An-Nisaa
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا يَحِلُّ لَكُمۡ أَن تَرِثُواْ ٱلنِّسَآءَ كَرۡهٗاۖ وَلَا تَعۡضُلُوهُنَّ لِتَذۡهَبُواْ بِبَعۡضِ مَآ ءَاتَيۡتُمُوهُنَّ إِلَّآ أَن يَأۡتِينَ بِفَٰحِشَةٖ مُّبَيِّنَةٖۚ وَعَاشِرُوهُنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ فَإِن كَرِهۡتُمُوهُنَّ فَعَسَىٰٓ أَن تَكۡرَهُواْ شَيۡـٔٗا وَيَجۡعَلَ ٱللَّهُ فِيهِ خَيۡرٗا كَثِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Sikovomerezedwa kwa inu kuwalowa chokolo akazi mowakakamiza. Ndipo musawaletse (kukwatiwa ndi amuna ena) ndi cholinga choti muwalande zina mwa zomwe mudawapatsa, (nkosaloledwa kutero) kupatula ngati atachita choipa choonekera. Ndipo khalani nawo mwa ubwino. Ngati mutawada (musalekane nawo), mwina mungade chinthu chomwe Allah waika zabwino zambiri mkati mwake.[116]
[116] Nthawi ya umbuli, chikhalidwe cha Arabu chidali chonchi:- Tate wa munthu akamwalira ana ake amamlowera chokolo akazi ake omwe sadabereke anawo. Mwana aliyense amalowa chokolo mwa mkazi watate wake yemwe sadali mayi wake wom’bala.
a) Akafuna kumkwatira adali kumtenga.
b) Ndipo akafuna kumkwatitsa kwa mwamuna wina, amamlamula ndalama mwamunayo iye natenga ndalamazo.
c) Kapena amangomuvutitsavutitsa kuti akafuna adziombole yekha pomlipira ndalama mwanayo.
d) Kapena amangommanga kuti asakwatiwenso mpaka imfa yake. Choncho apa Allah akuletsa machitidwe oipawa.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Versículo: (19) Surah: Suratu An-Nisaa
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar