የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (22) ምዕራፍ: ሱረቱ አል ሙጃደላ
لَّا تَجِدُ قَوۡمٗا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ يُوَآدُّونَ مَنۡ حَآدَّ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَلَوۡ كَانُوٓاْ ءَابَآءَهُمۡ أَوۡ أَبۡنَآءَهُمۡ أَوۡ إِخۡوَٰنَهُمۡ أَوۡ عَشِيرَتَهُمۡۚ أُوْلَٰٓئِكَ كَتَبَ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلۡإِيمَٰنَ وَأَيَّدَهُم بِرُوحٖ مِّنۡهُۖ وَيُدۡخِلُهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ رَضِيَ ٱللَّهُ عَنۡهُمۡ وَرَضُواْ عَنۡهُۚ أُوْلَٰٓئِكَ حِزۡبُ ٱللَّهِۚ أَلَآ إِنَّ حِزۡبَ ٱللَّهِ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Supeza anthu okhulupirira mwa Allah ndi tsiku lachimaliziro akukonda amene akutsutsana ndi Allah ndi Mthenga Wake, ngakhale atakhala atate awo, ana awo abale awo ndi akumtundu wawo; kwa iwo (Allah) wazika chikhulupiliro (champhamvu) m’mitima mwawo, ndipo wawalimbikitsa ndi mphamvu zochokera kwa Iye. Ndipo adzawalowetsa m’minda yomwe pansi pake pakuyenda mitsinje; adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Allah adzakondwera nawo ndipo (iwonso) adzakondwera Naye. Iwowa ndi chipani cha Allah. Dziwani kuti chipani cha Allah ndichopambana.[352]
[352] M’ndime imeneyi Allah akunenetsa kuti: ‘‘Amene akukhulupilira mwa Allah ndi tsiku lachimaliziro, asapalane ubwenzi ndi munthu wodana ndi Allah ndi Mthenga Wake ngakhale wodana ndi Allah yo atakhala bambo wake, mwana wake ndi wina aliyense; apatukane nawo ndithu; chifukwa kupanda kutero akusonyeza kufooka kwa chikhulupiliro. Mtumiki (s.a.w) adati: “Munthu adzakhala ndi amene amamkonda pa tsiku la chiweruziro.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም አንቀጽ: (22) ምዕራፍ: ሱረቱ አል ሙጃደላ
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት