Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Ayah: (22) Surah: Surah Al-Mujādilah
لَّا تَجِدُ قَوۡمٗا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ يُوَآدُّونَ مَنۡ حَآدَّ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَلَوۡ كَانُوٓاْ ءَابَآءَهُمۡ أَوۡ أَبۡنَآءَهُمۡ أَوۡ إِخۡوَٰنَهُمۡ أَوۡ عَشِيرَتَهُمۡۚ أُوْلَٰٓئِكَ كَتَبَ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلۡإِيمَٰنَ وَأَيَّدَهُم بِرُوحٖ مِّنۡهُۖ وَيُدۡخِلُهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ رَضِيَ ٱللَّهُ عَنۡهُمۡ وَرَضُواْ عَنۡهُۚ أُوْلَٰٓئِكَ حِزۡبُ ٱللَّهِۚ أَلَآ إِنَّ حِزۡبَ ٱللَّهِ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Supeza anthu okhulupirira mwa Allah ndi tsiku lachimaliziro akukonda amene akutsutsana ndi Allah ndi Mthenga Wake, ngakhale atakhala atate awo, ana awo abale awo ndi akumtundu wawo; kwa iwo (Allah) wazika chikhulupiliro (champhamvu) m’mitima mwawo, ndipo wawalimbikitsa ndi mphamvu zochokera kwa Iye. Ndipo adzawalowetsa m’minda yomwe pansi pake pakuyenda mitsinje; adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Allah adzakondwera nawo ndipo (iwonso) adzakondwera Naye. Iwowa ndi chipani cha Allah. Dziwani kuti chipani cha Allah ndichopambana.[352]
[352] M’ndime imeneyi Allah akunenetsa kuti: ‘‘Amene akukhulupilira mwa Allah ndi tsiku lachimaliziro, asapalane ubwenzi ndi munthu wodana ndi Allah ndi Mthenga Wake ngakhale wodana ndi Allah yo atakhala bambo wake, mwana wake ndi wina aliyense; apatukane nawo ndithu; chifukwa kupanda kutero akusonyeza kufooka kwa chikhulupiliro. Mtumiki (s.a.w) adati: “Munthu adzakhala ndi amene amamkonda pa tsiku la chiweruziro.”
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Ayah: (22) Surah: Surah Al-Mujādilah
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup