Check out the new design

የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - የቺቼዋኛ ትርጉም - ኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: አል ሙርሰላት   አንቀጽ:

Al-Mursalât

وَٱلۡمُرۡسَلَٰتِ عُرۡفٗا
Ndikulumbilira mphepo yomwe ikuomba motsatizana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱلۡعَٰصِفَٰتِ عَصۡفٗا
Ndi mphepo yamkuntho ikamakuntha.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَٱلنَّٰشِرَٰتِ نَشۡرٗا
Ndi mphepo yobalalitsa mitambo ndi mvula.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱلۡفَٰرِقَٰتِ فَرۡقٗا
Ndi ma Ayah osiyanitsa pakati pachoona ndi chonama;
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱلۡمُلۡقِيَٰتِ ذِكۡرًا
Ndi angelo opereka chivumbulutso kwa aneneri.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
عُذۡرًا أَوۡ نُذۡرًا
Kuti chichotse madandaulo kapena chikhale chenjezo;
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّمَا تُوعَدُونَ لَوَٰقِعٞ
Ndithu zimene mukulonjezedwa (kuti chimaliziro chidzakhalapo) zidzachitikadi (popanda chipeneko),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِذَا ٱلنُّجُومُ طُمِسَتۡ
Pamene nyenyezi zidzafafanizidwa (kuwala kwake ndi kuchotsedwa m’malo mwake).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ٱلسَّمَآءُ فُرِجَتۡ
Ndiponso pamene thambo lidzang‘ambidwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ٱلۡجِبَالُ نُسِفَتۡ
Ndi pamenenso mapiri adzachotsedwa m’malo mwake ndi kuperedwa (kukhala fumbi).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ٱلرُّسُلُ أُقِّتَتۡ
Ndi pamene atumiki adzasonkhanitsidwa pa nthawi yake, (kuti apereke umboni ku mibadwo yawo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لِأَيِّ يَوۡمٍ أُجِّلَتۡ
Kodi nditsiku lanji azichedwetsera (zinthu zikuluzikulu kuti zidzachitike)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لِيَوۡمِ ٱلۡفَصۡلِ
Nditsiku loweruza (pakati pa zolengedwa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِ
Nchiyani chingakudziwitse za tsiku la chiweruzirolo?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَلَمۡ نُهۡلِكِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Kodi sitidawaononge (anthu) akale (chifukwa cha machimo awo, monga anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ثُمَّ نُتۡبِعُهُمُ ٱلۡأٓخِرِينَ
Kenako titsatiza ena (okana Allah m’kuonongekako monga tidawachitira oyamba),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
كَذَٰلِكَ نَفۡعَلُ بِٱلۡمُجۡرِمِينَ
Chomwecho tiwachitiranso ochimwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: አል ሙርሰላት
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - የቺቼዋኛ ትርጉም - ኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ - የትርጉሞች ማዉጫ

ተርጓሙ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ።

መዝጋት