ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (59) سورة: آل عمران
إِنَّ مَثَلَ عِيسَىٰ عِندَ ٱللَّهِ كَمَثَلِ ءَادَمَۖ خَلَقَهُۥ مِن تُرَابٖ ثُمَّ قَالَ لَهُۥ كُن فَيَكُونُ
Ndithudi, fanizo la Isa (Yesu) kwa Allah lili ngati fanizo la Adam; adamulenga ndi dothi namuuza kuti: “Khala munthu.” Ndipo adakhaladi.[72]
[72] (Ndime 59-62) Ndime izi zidavumbulutsidwa pamene nthumwi za Chikhirisitu zidadza kwa Mtumiki (s.a.w) kuchokera ku Najirani. Iwowo adakangana ndi Mtumiki wa Allah pa nkhani ya Isa (Yesu). Iwo adati kwa Mtumiki wa Allah: “Bwanji iwe ukutukwana Mneneri wathu?” Iye adati: “Kodi ndikutukwana chotani?” Iwo adati: “Iwe ukuti iyeyo ndikapolo wa Allah.” Iye adati: “Inde. Iyeyo ndi kapolo wa Allah ndiponso mawu ake omwe adawaponya mwa namwali.’ Zitatero iwo adapsa mtima ndipo anakwiya nati: “Kodi iwe udamuonapo munthu wobadwa popanda tate? Ngati ukunenadi zoona tationetsa munthu wotere.” Apa mpomwe Allah adavumbulutsa ndime yakuti “Ndithudi, fanizo la Isa (Yesu) kwa Allah lili ngati fanizo la Adam”. Kenako anawaitanira ku Chisilamu. Iwo adati: “Tidalowa kale m’Chisilamu iwe usanadze.” Mtumiki (s.a.w) adati: “Mwanama. Pali zinthu zitatu zikukuletsani kulowa m’Chisilamu:
(a) Kunena kwanu mawu oti Allah wadzipangira mwana.
(b) Kudya kwanu nyama ya nkhumba.
(c) Kulambira kwanu mtanda.”
Pamene adapitiriza kumtsutsa mneneri Muhammad (s.a.w) adawapempha kuti atembelerane ponena kuti: “E Ambuye Mulungu! Mtembelereni ndi kumlanga amene akunena zabodza mwa ife pa nkhani ya Isa (Yesu)! Pompo Mtumiki (s.a.w) adasonkhanitsa anthu ake. Koma iwo atakhala upo adagwirizana kuti asalole kuopa kuti chilango chingawatsikire. Potero zidadziwika kwa anthu kuti iwo ngabodza.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (59) سورة: آل عمران
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق