Amuna ndiayang’aniri pa akazi chifukwa choti Allah watukula ena pa ulemelero pamwamba pa ena, chifukwa cha chuma chawo chimene apereka. Choncho, akazi abwino ndi omwe ali omvera, odzisunga ngakhale amuna awo palibe pakuti Allah wawalamula kudzisunga. Ndipo akazi omwe mukuopa mnyozo wawo, achenjezeni; ndipo kenako achokereni pamphasa, (apo ayi), akwapuleni (kukwapula kosavulaza), koma ngati akukumverani, musawafunire njira yowavutitsira. Ndithu Allah ndi yemwe ali Wapamwamba, Wamkulu (kuposa inu nonse).[122]
[122] Apa akuti amuna ndi amene akhale ndi ulamuliro pa akazi awo, powatsogolera ku miyambo yabwino. Osati kuti mkazi adzitukumule kwa mwamuna wake poti iye ngophunzira zedi kapena wanzeru zochuluka kotero kuti mwamuna m’nyumba osamuyesa kanthu. Ngati atero ndiye kuti sakhala Asilamu owona. M’ndimeyi atchulamonso makhalidwe ofunika kuti akazi akhale nawo. Ndipo atchulamo malangizo olangira nawo mkazi ngati samvera. Choyamba amchenjeze ndi mawu. Ngati kuchenjezako sikunathandize, asagone naye limodzi pamphasa. Ndipo ngati akupitirizabe kuchita mnyozo akupatsidwa chilolezo mwamuna kuti amlange pommenya mwakumuopyeza, osati kumenya komgulula nako mano. Komabe mahadisi a Mtumiki (s.a.w) akunena kuti asanaganize zommenya ayeseyese kumkonza ponena naye mofewa ndi kumuonetsa kulakwa kwake. Ngati atalephera zonsezi, aitane anthu kuti adzawayanjanitse m’njira yabwino. Naonso anthuwo akhale ndi cholinga choyanjanitsa osati kupasula. Amunanso akuwachenjeza apa kuti iwo ndi amene ali ndi nyonga ndi udindo. Allah ndiye Wamkulu kuposa iwo amunawo. Mawu oti “Hafizatu Lilighaibi” maulama ena akuwatanthauzira kuti “Akhale osunga chinsinsi,” chimene chili pakati pa iwo ndi amuna awo ndi zonse zomwe zimachitika m’nyumba, pakuti nthawi zambiri akazi sakhalira kuulula za m’nyumba.
Ndipo mpembedzeni Allah, ndipo musamphatikize ndi chilichonse; ndipo achitireni zabwino makolo awiri, ndi achibale, ndi ana amasiye ndi masikini ndi mnansi woyandikana naye nyumba, ndi wapadera wogundizana naye nyumba, ndi mnzako wokhala naye limodzi, ndi wapaulendo yemwe alibe choyendera, ndi omwe manja anu akumanja apeza (adzakazi). Ndithudi, Allah sakonda wodzitukumula ndi wodzitama.[123]
[123] M’ndime iyi akuwalamula anthu kuti apembedze Allah yekha ndi kumpempha Iye Yekha. Asapembedzenso china chilichonse, chamoyo kapena chakufa. Ndikuti awachitire zabwino makolo ake ndi onse amene awatchula m’ndimeyi. Sibwino kuthandiza anthu akumbali pomwe anthu omwe uli nawo pafupi sunawathandizepo.
4. إبقاء معلومات نسخة الترجمة الموجودة داخل المستند.
5. إفادة المصدر (QuranEnc.com) بأي ملاحظة على الترجمة.
6. تطوير الترجمات وفق النسخ الجديدة الصادرة من المصدر (QuranEnc.com).
7. عدم تضمين إعلانات لا تليق بترجمات معاني القرآن الكريم عند العرض.
نتائج البحث:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".