ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (51) سورة: النساء
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ أُوتُواْ نَصِيبٗا مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِ يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡجِبۡتِ وَٱلطَّٰغُوتِ وَيَقُولُونَ لِلَّذِينَ كَفَرُواْ هَٰٓؤُلَآءِ أَهۡدَىٰ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ سَبِيلًا
Kodi sukuwaona omwe apatsidwa gawo la nzeru zozindikira buku (la Allah)? Amakhulupirira mafano ndi asatana, ndipo akumati kwa amene sadakhulupirire: “Awa ali panjira yoongoka kwabasi kuposa okhulupirira (Asilamu).”[127]
[127] Mawu oti “Jibti ndi Twaghut’’ amanena za chinthu chomwe anthu akuchipembedza chamoyo kapena chakufa chomwe sichili Mulungu weniweni monga momwe lilili dzina loti Shaytan. Iloli limatchulidwa kwa aliyense amene akusokeretsa anthu ku njira ya Allah. Chifukwa cha kuipidwa ndi Asilamu, Ayuda adapita ku Makka kukapalana ubwenzi ndi Aquraish ndi Arabu ena opembedza mafano kuti athandizane nawo kumthira nkhondo Mtumiki Muhammad (s.a.w) pamodzi ndi omtsatira ake kuti achithetseretu chipembedzo cha Chisilamu. Choncho akuluakulu a Chiyuda atafika ku Makka adagwadira mafano ncholinga chofuna kukondweretsa Aquraish pomwe Ayudawo adali eni mabuku omwe salola kupembedza mafano. Adawalimbikitsanso Aquraish aja powauza kuti: “Zochita zanu pa chipembedzo chanu nzabwino kuposa zochita za Muhammad pachipembedzo chake chimene wadza nacho.” Iwo amanena izi akudziwa kuti akunama. Cholinga chawo kudali kupeza chithandizo kwa iwo kuti athetse Chisilamu chifukwa chakudzadzidwa ndi njiru m’mitima mwawo ponena kuti: “Nchotani kuti Muhammad (s.a.w) alandire chisomo chauneneri?” Iwo ankachita izi ngati kuti ufumu wa Allah udali m’manja mwawo kuti iwo ndi amene amagawa zachifundo cha Allah, chonsecho, Allah amapereka kwa yemwe wamfuna. Iye amachita chimene wafuna. Safunsidwa ndi aliyense pa chimene wachita. Koma iwo amafunsidwa.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (51) سورة: النساء
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق