للإطلاع على الموقع بحلته الجديدة

ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني سورة: الذاريات   آية:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلۡحُبُكِ
Ndikulumbilira thambo lomwe njira zake zambiri nzoikidwa mwaluso.
التفاسير العربية:
إِنَّكُمۡ لَفِي قَوۡلٖ مُّخۡتَلِفٖ
Ndithu inu muli m’mau otsutsana, (pa zimene mukunena).
التفاسير العربية:
يُؤۡفَكُ عَنۡهُ مَنۡ أُفِكَ
(Kupyolera m’mawu amenewa) akuchotsedwa ku icho (chikhulupiliro chalonjezo loona) amene adachotsedwa (ku chikhulupilirocho).
التفاسير العربية:
قُتِلَ ٱلۡخَرَّٰصُونَ
Aonongeka abodza (amene akunena za tsiku lachiweruziro mongoganizira.)
التفاسير العربية:
ٱلَّذِينَ هُمۡ فِي غَمۡرَةٖ سَاهُونَ
Iwo amene akubira mu umbuli, osalabadira (za tsiku lachimaliziro).
التفاسير العربية:
يَسۡـَٔلُونَ أَيَّانَ يَوۡمُ ٱلدِّينِ
Akufunsa (mwachipongwe ponena kuti) “Lidzakhala liti tsiku lamalipiro?”
التفاسير العربية:
يَوۡمَ هُمۡ عَلَى ٱلنَّارِ يُفۡتَنُونَ
(Limenelo ndi) tsiku lomwe iwo adzalangidwa ku Moto.
التفاسير العربية:
ذُوقُواْ فِتۡنَتَكُمۡ هَٰذَا ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تَسۡتَعۡجِلُونَ
(Adzawauza kuti): “Lawani chilango chanu ichi chimene munkachifulumizitsa (kuti chikufikeni).”
التفاسير العربية:
إِنَّ ٱلۡمُتَّقِينَ فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٍ
Ndithu oopa (Allah) adzakhala (akusangalala) m’minda ndi mu akasupe okongola,
التفاسير العربية:
ءَاخِذِينَ مَآ ءَاتَىٰهُمۡ رَبُّهُمۡۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَبۡلَ ذَٰلِكَ مُحۡسِنِينَ
Uku akulandira zimene wawapatsa Mbuye wawo (malipiro aulemu); ndithu iwo ankachita zabwino asanapeze izi.
التفاسير العربية:
كَانُواْ قَلِيلٗا مِّنَ ٱلَّيۡلِ مَا يَهۡجَعُونَ
Nthawi yausiku amagona pang’ono. (Amadzuka nachita mapemphero mochulukitsa).
التفاسير العربية:
وَبِٱلۡأَسۡحَارِ هُمۡ يَسۡتَغۡفِرُونَ
Ndipo kum’bandakucha, iwo amapempha chikhululuko,
التفاسير العربية:
وَفِيٓ أَمۡوَٰلِهِمۡ حَقّٞ لِّلسَّآئِلِ وَٱلۡمَحۡرُومِ
Ndipo m’chuma chawo mudali gawo (lodziwika) la opempha ndi osapempha (mwa osauka).
التفاسير العربية:
وَفِي ٱلۡأَرۡضِ ءَايَٰتٞ لِّلۡمُوقِنِينَ
M’nthaka muli zizindikiro kwa otsimikiza, (zosonyeza kuti Allah alipo).
التفاسير العربية:
وَفِيٓ أَنفُسِكُمۡۚ أَفَلَا تُبۡصِرُونَ
Ndi mwa inu nomwe; kodi simuona?
التفاسير العربية:
وَفِي ٱلسَّمَآءِ رِزۡقُكُمۡ وَمَا تُوعَدُونَ
Ndipo kumwamba kuli zokuthandizani (pa moyo wanu), ndi zimene mukulonjezedwa.
التفاسير العربية:
فَوَرَبِّ ٱلسَّمَآءِ وَٱلۡأَرۡضِ إِنَّهُۥ لَحَقّٞ مِّثۡلَ مَآ أَنَّكُمۡ تَنطِقُونَ
Ndikulumbilira Mbuye wa kumwamba ndi pansi, ndithu zimenezo ndi zoona monga kulili kuyankhula kwanu.
التفاسير العربية:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ضَيۡفِ إِبۡرَٰهِيمَ ٱلۡمُكۡرَمِينَ
Kodi yakufika nkhani ya alendo a Ibrahim; (angelo) olemekezeka?
التفاسير العربية:
إِذۡ دَخَلُواْ عَلَيۡهِ فَقَالُواْ سَلَٰمٗاۖ قَالَ سَلَٰمٞ قَوۡمٞ مُّنكَرُونَ
Pamene adalowa kwa iye ndi kunena kuti: “Salaam,” (“Mtendere”)! Iye adayankha: “Salaam,” (“Mtendere) inu ndinu anthu osadziwika (achilendo).”
التفاسير العربية:
فَرَاغَ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ فَجَآءَ بِعِجۡلٖ سَمِينٖ
Adatembenukira kwa akunyumba ake (mwakachetechete), ndipo adadza ndi nyama ya mwana wa ng’ombe yonona (yowotcha).
التفاسير العربية:
فَقَرَّبَهُۥٓ إِلَيۡهِمۡ قَالَ أَلَا تَأۡكُلُونَ
Naipereka kwa iwo (koma sadadye); iye adanena (modabwa): “Kodi bwanji simukudya?”
التفاسير العربية:
فَأَوۡجَسَ مِنۡهُمۡ خِيفَةٗۖ قَالُواْ لَا تَخَفۡۖ وَبَشَّرُوهُ بِغُلَٰمٍ عَلِيمٖ
Mumtima mwake adadzazidwa mantha ndi iwo. Iwo adati: “Usaope,” ndipo adamuuza nkhani yabwino ya kubala mwana wodziwa.
التفاسير العربية:
فَأَقۡبَلَتِ ٱمۡرَأَتُهُۥ فِي صَرَّةٖ فَصَكَّتۡ وَجۡهَهَا وَقَالَتۡ عَجُوزٌ عَقِيمٞ
Adadza mkazi wake ndi mkuwe (pamene adamva nkhani yabwino ija). Adadzimenya kunkhope (ndi dzanja lake kusonyeza kudabwa ndi kusatheka). Ndipo adati: (“Ine ndine) nkhalamba (ndiponso) chumba; (ndingabereke bwanji)?”
التفاسير العربية:
قَالُواْ كَذَٰلِكِ قَالَ رَبُّكِۖ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡحَكِيمُ ٱلۡعَلِيمُ
Iwo adati: “Momwemo, Mbuye wako wanena. Iye Ngwanzeru zakuya (pa chilichonse chimene akulamula); Ngodziwa; (palibe chimene chingabisike kwa Iye).
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني سورة: الذاريات
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا - فهرس التراجم

ترجمها خالد إبراهيم بيتالا.

إغلاق