ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (136) سورة: الأنعام
وَجَعَلُواْ لِلَّهِ مِمَّا ذَرَأَ مِنَ ٱلۡحَرۡثِ وَٱلۡأَنۡعَٰمِ نَصِيبٗا فَقَالُواْ هَٰذَا لِلَّهِ بِزَعۡمِهِمۡ وَهَٰذَا لِشُرَكَآئِنَاۖ فَمَا كَانَ لِشُرَكَآئِهِمۡ فَلَا يَصِلُ إِلَى ٱللَّهِۖ وَمَا كَانَ لِلَّهِ فَهُوَ يَصِلُ إِلَىٰ شُرَكَآئِهِمۡۗ سَآءَ مَا يَحۡكُمُونَ
Ampangira Allah (amugawira) gawo m’zomera ndi ziweto zimene (Allah) adalenga. Akunena: “Gawo ili ndi la Allah.” Mkuyankhula kwawo kwachabe: “Ndipo gawo ili ndi la aja omwe tikuwaphatikiza ndi Allah.” Choncho zomwe alinga kuwapatsa aphatikizi awo, sizingafike kwa Allah. Ndipo zimene zili za Allah, ndizomwe zingafike kwa aphatikizi awo (mafano awo). Kwaipitsitsa kuweruza kwaoku.[174]
[174] Kale anthu osakhulupilira pamene ankalima akafuna kubzala, minda yawo adali kuigawa zigawo ziwiri. Ankati: ‘‘Mbewu za chigawo ichi nza Allah, kuti mbewu zakezo adzazigwiritsa ntchito powapatsa masikini, ana a masiye ndi osowa. Ndipo ankatinso: “Mbewu za gawo ili nzamafano athu omwe ankati ngamnzake a Allah kuti zinthu zotuluka m’menemo ziperekedwe kwa anthu ogwira ntchito m’menemo. Choncho ngati patapezeka mliri pachigawo chomwe ankati zokolola zake nzamafano awo, amatenga chigawo chomwe amati dzinthu dzake nza Allah napereka ku mafano. Koma mliri ukagwera pa chigawo cha Allah, sadali kutenga zamafano nkupereka kwa Allah. Izi amachita ngati mafano ngabwino kuposa Allah.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (136) سورة: الأنعام
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق