《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (136) 章: 艾奈尔姆
وَجَعَلُواْ لِلَّهِ مِمَّا ذَرَأَ مِنَ ٱلۡحَرۡثِ وَٱلۡأَنۡعَٰمِ نَصِيبٗا فَقَالُواْ هَٰذَا لِلَّهِ بِزَعۡمِهِمۡ وَهَٰذَا لِشُرَكَآئِنَاۖ فَمَا كَانَ لِشُرَكَآئِهِمۡ فَلَا يَصِلُ إِلَى ٱللَّهِۖ وَمَا كَانَ لِلَّهِ فَهُوَ يَصِلُ إِلَىٰ شُرَكَآئِهِمۡۗ سَآءَ مَا يَحۡكُمُونَ
Ampangira Allah (amugawira) gawo m’zomera ndi ziweto zimene (Allah) adalenga. Akunena: “Gawo ili ndi la Allah.” Mkuyankhula kwawo kwachabe: “Ndipo gawo ili ndi la aja omwe tikuwaphatikiza ndi Allah.” Choncho zomwe alinga kuwapatsa aphatikizi awo, sizingafike kwa Allah. Ndipo zimene zili za Allah, ndizomwe zingafike kwa aphatikizi awo (mafano awo). Kwaipitsitsa kuweruza kwaoku.[174]
[174] Kale anthu osakhulupilira pamene ankalima akafuna kubzala, minda yawo adali kuigawa zigawo ziwiri. Ankati: ‘‘Mbewu za chigawo ichi nza Allah, kuti mbewu zakezo adzazigwiritsa ntchito powapatsa masikini, ana a masiye ndi osowa. Ndipo ankatinso: “Mbewu za gawo ili nzamafano athu omwe ankati ngamnzake a Allah kuti zinthu zotuluka m’menemo ziperekedwe kwa anthu ogwira ntchito m’menemo. Choncho ngati patapezeka mliri pachigawo chomwe ankati zokolola zake nzamafano awo, amatenga chigawo chomwe amati dzinthu dzake nza Allah napereka ku mafano. Koma mliri ukagwera pa chigawo cha Allah, sadali kutenga zamafano nkupereka kwa Allah. Izi amachita ngati mafano ngabwino kuposa Allah.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (136) 章: 艾奈尔姆
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭