(Kuti): “Mponye (mwanayo) m’bokosi ndipo ponya bokosilo mu mtsinje; ndipo mtsinje umponya m’mbali kuti amtenge mdani wanga ndi mdani wake (ndi kuti aleredwe mwaubwino ndi Farawo); ndipo ndidaika kukondeka pa iwe kochokera kwa Ine (kuti ukhale wokondedwa ndi anthu onse) ndikuti uleredwe moyang’aniridwa ndi Ine.”
(Kumbuka) pomwe mlongo wako ankayenda (kunka kubanja la Farawo) Ndipo adati: “Kodi ndikulondolereni munthu amene angathe kumlera?” Ndipo tidakubwezera kwa mayi wako kuti maso ake atonthole, ndipo asadandaule. Ndipo kenaka udapha munthu (mwangozi), ndipo tidakupulumutsa ku madandaulo; tidakuyesa ndi mayeso ambiri. Udakhala zaka zambiri ndi anthu a ku Madiyan. Kenaka wabwera (apa) monga mwachikonzero, E, iwe Mûsa![279]
[279] Omasulira adati: Pamene adamtola Musa akubanja la Farawo sadali kuyamwa bele la mkazi aliyense, amakana, chifukwa Allah adamuletsa kuyamwa mawere aakazi ena oyamwitsa. Ndipo mayi wake adali ndi madandaulo ndi chisoni atamponya mumtsinje, ndipo adamulamula mlongo wake kunka nafufuza za mwanayo. Pamene adafika kunyumba ya Farawo, adamuona. Adati: “Kodi ndikulondolereni mkazi wokhulupirika, waulemu kuti azikuyamwitsirani mwanayo?” Ndipo iwo adati: “Pita kamtenge.” Choncho adadza ndi mayi wa Musa. Pamene adatulutsa bere lake, Musa adayamwa. Choncho mkazi wa Farawo adasangalala kwabasi namuuza make Musa: “Dzikhala pamodzi nane kunyumba yachifumu.” Iye adati: “Sindingathe kusiya nyumba yanga ndi ana anga. Koma ndimtenga ndipo ndikhala ndikudza naye nthawi iliyonse ukamufuna.” Mkazi wa Farawo adavomereza ndi kumchitira zabwino mayiyo. Ili ndilo tanthauzo la mawu a Allah akuti: “Tidakubwezera kwa mayi wako kuti diso lake litonthole, asadandaule.”
Choncho mpitireni, ndikumuuza (kuti): “Ndithu ife ndife atumiki a Mbuye wako. Asiye ana a Israyeli achoke ndi ife, ndipo usawazunze; ndithu takudzera ndi chozizwitsa chochokera kwa Mbuye wako (chomwe ndi mboni yathu pa zomwe tikukuuzazi), ndipo mtendere ukhala pa yemwe atsate chiwongoko.”
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
অনুসন্ধানৰ ফলাফল:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".