Check out the new design

Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Khaled Ibrahim Batyala * - Translations’ Index


Translation of the meanings Surah: Tā-ha   Ayah:
إِذۡ أَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰٓ أُمِّكَ مَا يُوحَىٰٓ
“Pamene mayi wako tidamuzindikiritsa zimene tidamzindikiritsa (kuti azichite).”
Arabic explanations of the Qur’an:
أَنِ ٱقۡذِفِيهِ فِي ٱلتَّابُوتِ فَٱقۡذِفِيهِ فِي ٱلۡيَمِّ فَلۡيُلۡقِهِ ٱلۡيَمُّ بِٱلسَّاحِلِ يَأۡخُذۡهُ عَدُوّٞ لِّي وَعَدُوّٞ لَّهُۥۚ وَأَلۡقَيۡتُ عَلَيۡكَ مَحَبَّةٗ مِّنِّي وَلِتُصۡنَعَ عَلَىٰ عَيۡنِيٓ
(Kuti): “Mponye (mwanayo) m’bokosi ndipo ponya bokosilo mu mtsinje; ndipo mtsinje umponya m’mbali kuti amtenge mdani wanga ndi mdani wake (ndi kuti aleredwe mwaubwino ndi Farawo); ndipo ndidaika kukondeka pa iwe kochokera kwa Ine (kuti ukhale wokondedwa ndi anthu onse) ndikuti uleredwe moyang’aniridwa ndi Ine.”
Arabic explanations of the Qur’an:
إِذۡ تَمۡشِيٓ أُخۡتُكَ فَتَقُولُ هَلۡ أَدُلُّكُمۡ عَلَىٰ مَن يَكۡفُلُهُۥۖ فَرَجَعۡنَٰكَ إِلَىٰٓ أُمِّكَ كَيۡ تَقَرَّ عَيۡنُهَا وَلَا تَحۡزَنَۚ وَقَتَلۡتَ نَفۡسٗا فَنَجَّيۡنَٰكَ مِنَ ٱلۡغَمِّ وَفَتَنَّٰكَ فُتُونٗاۚ فَلَبِثۡتَ سِنِينَ فِيٓ أَهۡلِ مَدۡيَنَ ثُمَّ جِئۡتَ عَلَىٰ قَدَرٖ يَٰمُوسَىٰ
(Kumbuka) pomwe mlongo wako ankayenda (kunka kubanja la Farawo) Ndipo adati: “Kodi ndikulondolereni munthu amene angathe kumlera?” Ndipo tidakubwezera kwa mayi wako kuti maso ake atonthole, ndipo asadandaule. Ndipo kenaka udapha munthu (mwangozi), ndipo tidakupulumutsa ku madandaulo; tidakuyesa ndi mayeso ambiri. Udakhala zaka zambiri ndi anthu a ku Madiyan. Kenaka wabwera (apa) monga mwachikonzero, E, iwe Mûsa![279]
[279] Omasulira adati: Pamene adamtola Musa akubanja la Farawo sadali kuyamwa bele la mkazi aliyense, amakana, chifukwa Allah adamuletsa kuyamwa mawere aakazi ena oyamwitsa. Ndipo mayi wake adali ndi madandaulo ndi chisoni atamponya mumtsinje, ndipo adamulamula mlongo wake kunka nafufuza za mwanayo. Pamene adafika kunyumba ya Farawo, adamuona. Adati: “Kodi ndikulondolereni mkazi wokhulupirika, waulemu kuti azikuyamwitsirani mwanayo?” Ndipo iwo adati: “Pita kamtenge.” Choncho adadza ndi mayi wa Musa. Pamene adatulutsa bere lake, Musa adayamwa. Choncho mkazi wa Farawo adasangalala kwabasi namuuza make Musa: “Dzikhala pamodzi nane kunyumba yachifumu.” Iye adati: “Sindingathe kusiya nyumba yanga ndi ana anga. Koma ndimtenga ndipo ndikhala ndikudza naye nthawi iliyonse ukamufuna.” Mkazi wa Farawo adavomereza ndi kumchitira zabwino mayiyo. Ili ndilo tanthauzo la mawu a Allah akuti: “Tidakubwezera kwa mayi wako kuti diso lake litonthole, asadandaule.”
Arabic explanations of the Qur’an:
وَٱصۡطَنَعۡتُكَ لِنَفۡسِي
Ndipo ndakusankha ndekha (kuti ukhale Mtumiki Wanga).
Arabic explanations of the Qur’an:
ٱذۡهَبۡ أَنتَ وَأَخُوكَ بِـَٔايَٰتِي وَلَا تَنِيَا فِي ذِكۡرِي
Pita iwe ndi m’bale wako ndi zozizwitsa Zanga, ndipo musatope (musasiye) kundikumbukira.
Arabic explanations of the Qur’an:
ٱذۡهَبَآ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ إِنَّهُۥ طَغَىٰ
Pitani kwa Farawo, ndithu iye wapyola malire.
Arabic explanations of the Qur’an:
فَقُولَا لَهُۥ قَوۡلٗا لَّيِّنٗا لَّعَلَّهُۥ يَتَذَكَّرُ أَوۡ يَخۡشَىٰ
Kamuuzeni mawu ofewa mwina akalingalira (uthengawo) kapena akaopa.
Arabic explanations of the Qur’an:
قَالَا رَبَّنَآ إِنَّنَا نَخَافُ أَن يَفۡرُطَ عَلَيۡنَآ أَوۡ أَن يَطۡغَىٰ
(Iwo) adati: “Mbuye wathu ndithu ife tikuopa kuti angatimbwandire kapena kutipyolera malire (tisananene kanthu).”
Arabic explanations of the Qur’an:
قَالَ لَا تَخَافَآۖ إِنَّنِي مَعَكُمَآ أَسۡمَعُ وَأَرَىٰ
(Allah) adati: “Musaope. Ndithu Ine ndili nanu pamodzi. ndikumva, ndiponso ndikuona.”
Arabic explanations of the Qur’an:
فَأۡتِيَاهُ فَقُولَآ إِنَّا رَسُولَا رَبِّكَ فَأَرۡسِلۡ مَعَنَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ وَلَا تُعَذِّبۡهُمۡۖ قَدۡ جِئۡنَٰكَ بِـَٔايَةٖ مِّن رَّبِّكَۖ وَٱلسَّلَٰمُ عَلَىٰ مَنِ ٱتَّبَعَ ٱلۡهُدَىٰٓ
Choncho mpitireni, ndikumuuza (kuti): “Ndithu ife ndife atumiki a Mbuye wako. Asiye ana a Israyeli achoke ndi ife, ndipo usawazunze; ndithu takudzera ndi chozizwitsa chochokera kwa Mbuye wako (chomwe ndi mboni yathu pa zomwe tikukuuzazi), ndipo mtendere ukhala pa yemwe atsate chiwongoko.”
Arabic explanations of the Qur’an:
إِنَّا قَدۡ أُوحِيَ إِلَيۡنَآ أَنَّ ٱلۡعَذَابَ عَلَىٰ مَن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ
“Ndithu zavumbulutsidwa kwa ife kuti chilango chiwapeza amene akutsutsa (zimenezi) ndikuzitembenukira kumbali.”
Arabic explanations of the Qur’an:
قَالَ فَمَن رَّبُّكُمَا يَٰمُوسَىٰ
(Farawo) adati: “Kodi Mbuye wanu ndani, iwe Mûsa?”
Arabic explanations of the Qur’an:
قَالَ رَبُّنَا ٱلَّذِيٓ أَعۡطَىٰ كُلَّ شَيۡءٍ خَلۡقَهُۥ ثُمَّ هَدَىٰ
(Mûsa) adati: “Mbuye wathu ndi yemwe adapatsa chinthu chilichonse chilengedwe chake, kenako adachiongolera (kutsata chimene chikulingana ndi chilengedwe chake).”
Arabic explanations of the Qur’an:
قَالَ فَمَا بَالُ ٱلۡقُرُونِ ٱلۡأُولَىٰ
(Farawo) adati: “Nanga mibadwo yakale ili bwanji, (imene idapita iwe usadadze?”)
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Surah: Tā-ha
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Khaled Ibrahim Batyala - Translations’ Index

Translated by Khalid Ibrahim Betala

close