Ndithu nthawi ya tsiku lachimaliziro idza; (choncho ikonzekere ndi ntchito zabwino); ndikuibisa dala (kwa anthu) kuti mzimu uliwonse udzalipidwe zimene udachita.[274]
[274] Womasulira Qur’an adati cholinga chakubisa kudza kwa tsiku la chimaliziro, ndi nthawi ya imfa ya munthu ndikuti Allah wapamwambamwamba adalamula kuti sangavomereze kulapa tsiku la chimaliziro litadza, ndi nthawi ya imfa itamufikira munthu. Anthu akadadziwa nthawi yeniyeni ya chimaliziro ndi nthawi yakudza kwa imfa yawo, akadakhala akuchita zinthu zoyipa naakhala ndi chiyembekezero choti adzalapa nthawi ikayandikira, nadzapulumuka kuchilango cha Allah. Koma Allah anabisa zimenezo kuti anthu akhale tcheru nthawi zonse ndikukhala okonzekera za imfa ndi za tsiku la chimaliziro kuti zingawadzere modzidzimutsa.
“Ndipo masulani mfundo yomwe ili ku lirime kwanga, (ndimasulireni kumangika kwa lirime langa kuti mawu anga akakhale opanda chibwibwi).”[278]
[278] Musa adali wachibwibwi koma chibwibwi chake sichinali chachibadwa. Kuyamba kwa chibwibwi chake kudali motere: Kumayambiliro amoyo wake adali kukhala m’nyumba ya Farawo. Ndipo nthawi ina Farawo adamuika pamiyendo yake iye ali mwana. Musa adakoka ndevu za Farawo ndi dzanja lake. Ndipo Farawo adakwiya natsimikiza zomupha. Ndipo Asiya, mkazi wake, adati kwa iye: “Iyeyu sazindikira. Ndipo ndikusonyeza zimenezo kuti udziwe.Yandikitsani kwa iye makala awiri ndi ngale ziwiri. Ngati atola ngalezo ndiye kuti akuzindikira. Koma akatola khala lamoto, apo uzindikira kuti ameneyu sazindikira kanthu. Choncho Farawo adamuyandikizira zonsezo ndipo iye adatola khala lamoto nkuliponya mkamwa mwake. Potero palirime lake padali kachipsera. Nkhaniyi ikupezeka m’buku la Tabariyi, volume 16 tsamba 159.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
Search results:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".