Check out the new design

Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: Tâ Hâ   Verset:
وَأَنَا ٱخۡتَرۡتُكَ فَٱسۡتَمِعۡ لِمَا يُوحَىٰٓ
Ndipo Ine ndakusankha (kuti ukhale Mtumiki); choncho mvera zonse zomwe zikuvumbulutsidwa (kwa iwe).
Les exégèses en arabe:
إِنَّنِيٓ أَنَا ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّآ أَنَا۠ فَٱعۡبُدۡنِي وَأَقِمِ ٱلصَّلَوٰةَ لِذِكۡرِيٓ
Ndithu Ine ndine Allah palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Ine; choncho ndipembeze, pemphera Swala moyenera pondikumbukira.
Les exégèses en arabe:
إِنَّ ٱلسَّاعَةَ ءَاتِيَةٌ أَكَادُ أُخۡفِيهَا لِتُجۡزَىٰ كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا تَسۡعَىٰ
Ndithu nthawi ya tsiku lachimaliziro idza; (choncho ikonzekere ndi ntchito zabwino); ndikuibisa dala (kwa anthu) kuti mzimu uliwonse udzalipidwe zimene udachita.[274]
[274] Womasulira Qur’an adati cholinga chakubisa kudza kwa tsiku la chimaliziro, ndi nthawi ya imfa ya munthu ndikuti Allah wapamwambamwamba adalamula kuti sangavomereze kulapa tsiku la chimaliziro litadza, ndi nthawi ya imfa itamufikira munthu. Anthu akadadziwa nthawi yeniyeni ya chimaliziro ndi nthawi yakudza kwa imfa yawo, akadakhala akuchita zinthu zoyipa naakhala ndi chiyembekezero choti adzalapa nthawi ikayandikira, nadzapulumuka kuchilango cha Allah. Koma Allah anabisa zimenezo kuti anthu akhale tcheru nthawi zonse ndikukhala okonzekera za imfa ndi za tsiku la chimaliziro kuti zingawadzere modzidzimutsa.
Les exégèses en arabe:
فَلَا يَصُدَّنَّكَ عَنۡهَا مَن لَّا يُؤۡمِنُ بِهَا وَٱتَّبَعَ هَوَىٰهُ فَتَرۡدَىٰ
Ndipo asakutsekereze (ku khulupirira) zimenezo yemwe saikhulupirira (Kiyamayo), ndipo akungotsata zilakolako za mtima wake; kuopa kuti Ungadzaonongeke.”
Les exégèses en arabe:
وَمَا تِلۡكَ بِيَمِينِكَ يَٰمُوسَىٰ
“Kodi nchiyani icho chili kudzanja Lako ladzanjadzanja, iwe Mûsa?”
Les exégèses en arabe:
قَالَ هِيَ عَصَايَ أَتَوَكَّؤُاْ عَلَيۡهَا وَأَهُشُّ بِهَا عَلَىٰ غَنَمِي وَلِيَ فِيهَا مَـَٔارِبُ أُخۡرَىٰ
(Mûsa) adati: “Iyi ndi ndodo yanga, ndimaitsamira (poyenda) ndi kuphopholera masamba a mbuzi zanga; ndiponso (m’ndodomo) muli zina zondithandiza.”[275]
[275] Womasulira adati yankho lakuti: “Iyi ndi ndodo yanga,” lidali yankho lokwana. Koma iye adaonjezera payankho mawu ena amene sadamufunse chifukwa chakuti pomwe adalipo padali pamalo poyenera kutambasula mawu pakuti Allah ndiye adali kuyankhula naye popanda mkhalapakati. Uku kudali kuti amve kukoma koyankhulana ndi Allah. Pajatu mawu a wokondedwa amatonthoza moyo ndipo amachotsa kutopa kwa mtundu uliwonse.
Les exégèses en arabe:
قَالَ أَلۡقِهَا يَٰمُوسَىٰ
(Allah) adati: “Iponye iwe Mûsa!”
Les exégèses en arabe:
فَأَلۡقَىٰهَا فَإِذَا هِيَ حَيَّةٞ تَسۡعَىٰ
Ndipo adaiponya; pompo idasanduka njoka yoyenda mothamanga. [276]
[276] Ibun Abbas adati ndodoyi idasanduka chinjoka chachimuna chomwe chidali kumeza miyala ndi mitengo. Pamene Musa adachiona chikumeza chilichonse adachiopa. Nkhaniyi ikupezeka m’buku la Qurtubi, volume 11, tsamba la 190.
Les exégèses en arabe:
قَالَ خُذۡهَا وَلَا تَخَفۡۖ سَنُعِيدُهَا سِيرَتَهَا ٱلۡأُولَىٰ
(Allah) adati: “Igwire, usaope. Tiibwezera m’chikhalidwe chake Choyamba.”
Les exégèses en arabe:
وَٱضۡمُمۡ يَدَكَ إِلَىٰ جَنَاحِكَ تَخۡرُجۡ بَيۡضَآءَ مِنۡ غَيۡرِ سُوٓءٍ ءَايَةً أُخۡرَىٰ
“Ndipo lipane dzanja lako m’khwapa mwako lituluka lili loyera (ngati kuwala kwadzuwa ndi mwezi). Osati mwamatenda, (ichi chikhala) chozizwitsa china.”[277]
[277] Ibun Kathiri adati Musa ankati akalilowetsa dzanjalo mkhwapa mwake kenako nkulitulutsa, limatuluka lili kung’anima ngati chiditswa chamwezi popanda chonyansa chilichonse. Ichi chidali china mwa zozizwitsa zake.
Les exégèses en arabe:
لِنُرِيَكَ مِنۡ ءَايَٰتِنَا ٱلۡكُبۡرَى
“Kuti tikusonyeze zina mwa zozizwitsa zathu, zazikuluzikulu.”
Les exégèses en arabe:
ٱذۡهَبۡ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ إِنَّهُۥ طَغَىٰ
“Pita kwa Farawo, ndithu iye wapyola malire.”
Les exégèses en arabe:
قَالَ رَبِّ ٱشۡرَحۡ لِي صَدۡرِي
(Mûsa) adati: “E Mbuye wanga! Nditsakulireni chifuwa changa.”
Les exégèses en arabe:
وَيَسِّرۡ لِيٓ أَمۡرِي
“Ndi kundifewetsera ntchito yangayi (imene mwandipatsa kuti uthengawu ndikaufalitse m’njira yoyenera).”
Les exégèses en arabe:
وَٱحۡلُلۡ عُقۡدَةٗ مِّن لِّسَانِي
“Ndipo masulani mfundo yomwe ili ku lirime kwanga, (ndimasulireni kumangika kwa lirime langa kuti mawu anga akakhale opanda chibwibwi).”[278]
[278] Musa adali wachibwibwi koma chibwibwi chake sichinali chachibadwa. Kuyamba kwa chibwibwi chake kudali motere: Kumayambiliro amoyo wake adali kukhala m’nyumba ya Farawo. Ndipo nthawi ina Farawo adamuika pamiyendo yake iye ali mwana. Musa adakoka ndevu za Farawo ndi dzanja lake. Ndipo Farawo adakwiya natsimikiza zomupha. Ndipo Asiya, mkazi wake, adati kwa iye: “Iyeyu sazindikira. Ndipo ndikusonyeza zimenezo kuti udziwe.Yandikitsani kwa iye makala awiri ndi ngale ziwiri. Ngati atola ngalezo ndiye kuti akuzindikira. Koma akatola khala lamoto, apo uzindikira kuti ameneyu sazindikira kanthu. Choncho Farawo adamuyandikizira zonsezo ndipo iye adatola khala lamoto nkuliponya mkamwa mwake. Potero palirime lake padali kachipsera. Nkhaniyi ikupezeka m’buku la Tabariyi, volume 16 tsamba 159.
Les exégèses en arabe:
يَفۡقَهُواْ قَوۡلِي
“Kuti (anthu) akamvetse mawu anga.”
Les exégèses en arabe:
وَٱجۡعَل لِّي وَزِيرٗا مِّنۡ أَهۡلِي
“Ndipo ndipatseni nduna (mthandizi) yochokera kubanja langa.”
Les exégèses en arabe:
هَٰرُونَ أَخِي
“M’bale wanga Harun.”
Les exégèses en arabe:
ٱشۡدُدۡ بِهِۦٓ أَزۡرِي
“Limbitsani nyonga zanga ndi iye.”
Les exégèses en arabe:
وَأَشۡرِكۡهُ فِيٓ أَمۡرِي
“Ndipo mphatikeni ku ntchito yangayi.”
Les exégèses en arabe:
كَيۡ نُسَبِّحَكَ كَثِيرٗا
“Kuti tikulemekezeni kwambiri.”
Les exégèses en arabe:
وَنَذۡكُرَكَ كَثِيرًا
“Ndi kukutamandani kwabasi.”
Les exégèses en arabe:
إِنَّكَ كُنتَ بِنَا بَصِيرٗا
“Ndithu inu (nthawi zonse) mumationa (ndi kutisunga).”
Les exégèses en arabe:
قَالَ قَدۡ أُوتِيتَ سُؤۡلَكَ يَٰمُوسَىٰ
(Allah) adati: “Ndithu wapatsidwa zomwe wapempha, E, iwe Mûsa.”
Les exégèses en arabe:
وَلَقَدۡ مَنَنَّا عَلَيۡكَ مَرَّةً أُخۡرَىٰٓ
“Ndipo ndithu tidakuchitira ubwino nthawi ina (popanda iwe kutipempha).”
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: Tâ Hâ
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ - Lexique des traductions

Traduit par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ.

Fermeture