Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: əl-İnşiqaq   Ayə:

əl-İnşiqaq

إِذَا ٱلسَّمَآءُ ٱنشَقَّتۡ
Pamene thambo lidzang’ambike (kusonyeza mapeto ake),
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَذِنَتۡ لِرَبِّهَا وَحُقَّتۡ
Ndikudzamvera lamulo la Mbuye wake; ndipo lidzayenera kutero,
Ərəbcə təfsirlər:
وَإِذَا ٱلۡأَرۡضُ مُدَّتۡ
Ndiponso pamene nthaka idzatambasulidwe (pogumuka mapiri ake ndikuchoka zitunda zake),
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَلۡقَتۡ مَا فِيهَا وَتَخَلَّتۡ
Ndi kutaya zomwe zidali mkati mwake ndi kukhala yopanda kanthu,[405]
[405] Chimodzi mwa zinthu zoopsa zomwe zidzachitika tsiku lachimaliziro ndi kugwedezeka kwa nthaka mwamphamvu zedi mpaka idzalekana ndi mapiri amene ali zichiri zake zoletsa kugwedezeka kwake. Pachifukwa ichi idzatambasuka ndipo zomwe zidali mkati mwake zidzatulukira pamtunda; nthaka idzangokhala yopanda kanthu mkati mwake.
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَذِنَتۡ لِرَبِّهَا وَحُقَّتۡ
Ndikudzamvera lamulo la Mbuye wake; ndipo lidzayenera kutero. (Choncho zikadzachitika zimenezi ndiye kuti munthu adzalandira mphoto ya zochita zake).[406]
[406] Allah pambuyo ponena zimenezi sadanene kuti chidzachitika chiyani. Alekera munthu mwini wake kuti aganizire chomwe chidzachitika zikadzapezeka zoopsa kuti aope kwambiri.
Ərəbcə təfsirlər:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡإِنسَٰنُ إِنَّكَ كَادِحٌ إِلَىٰ رَبِّكَ كَدۡحٗا فَمُلَٰقِيهِ
E iwe munthu! Ndithudi iwe ukubwerera kwa Mbuye wako (ndi zochita zako zabwino kapena zoipa), kubwerera kotsimikizika, ndipo iwe ukumana (ndi zotsatira za zochitachita zako).
Ərəbcə təfsirlər:
فَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِيَمِينِهِۦ
Tsono amene adzapatsidwe kaundula wa zochita zake kudzanja la manja,[407]
[407] Tsiku la chiweruziro munthu adzapatsidwa kaundula wake monga momwe zanenedwa mu Ayah 10 Surah Takwir, choncho ena adzapatsidwa ndi dzanja la kumanja; iwo ndiwo anthu abwino. Pomwe ena adzapatsidwa ndi dzanja la kumanzere, chakumbali yakumsana; iwowo ndiwo anthu oipa.
Ərəbcə təfsirlər:
فَسَوۡفَ يُحَاسَبُ حِسَابٗا يَسِيرٗا
Basi iye, adzawerengedwa, kuwerengedwa kopepuka,[408]
[408] Anthu ena adzawerengedwa popanda kufunsidwa mafunso pa zimene adachita, koma adzangowauza zabwino zawo ndi zoipa zawo ndipo pambuyo pake adzawakhululukira zoipazo ndi kudzawalipira pa zabwinozo. Iwowa ndiwo anthu abwino; chimenechi ndicho chiweruzo chofewa. Ena adzaweruzidwa pofunsidwa pa chilichonse m’zimene ankachita monga kuti “Bwanji ichi udachita? Bwanji ichi sudachite”? Iwowa ndiwo anthu oipa; chiwerengero chawo chidzakhala chokhwima.
Ərəbcə təfsirlər:
وَيَنقَلِبُ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ مَسۡرُورٗا
Ndipo adzabwerera kwa anthu ake (okhulupirira) ali wokondwa.
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ وَرَآءَ ظَهۡرِهِۦ
Koma yemwe adzapatsidwe kaundula wa zochita zake chakumanzere kudzera kumbuyo kwa msana wake (chifukwa chomunyoza),
Ərəbcə təfsirlər:
فَسَوۡفَ يَدۡعُواْ ثُبُورٗا
Basi, iye adzaitana imfa (kuti imufikire; kuti afe apumule, koma siidzamufikira);
Ərəbcə təfsirlər:
وَيَصۡلَىٰ سَعِيرًا
Ndipo adzalowa ku Moto woyaka.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّهُۥ كَانَ فِيٓ أَهۡلِهِۦ مَسۡرُورًا
Kamba kakuti iye adali wokondwa; (kukondwa kwa machimo) pamodzi ndi anthu ake (osaganizira za mathero ake).
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّهُۥ ظَنَّ أَن لَّن يَحُورَ
Ndithudi, amaganiza kuti sadzabwerera (kwa Allah ndiponso sadzawerengedwa).
Ərəbcə təfsirlər:
بَلَىٰٓۚ إِنَّ رَبَّهُۥ كَانَ بِهِۦ بَصِيرٗا
Chifukwa ninji (asabwelere)? Ndithu Mbuye wake adali kumuona. (Choncho alipidwa zimene adachita).
Ərəbcə təfsirlər:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِٱلشَّفَقِ
Choncho ndikulumbilira kufiira kwa dzuwa (pamene likulowa).
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱلَّيۡلِ وَمَا وَسَقَ
Ndi usiku ndi zimene wasonkhanitsa,[409]
[409] Kubalalikana masana ndi chizolowezi cha anthu ndi nyama chifukwa chofunafuna zinthu zothandiza pa moyo wawo. Tsono usiku ukabwera amasonkhana ndi kukhala pamodzi. Ndipo ili ndilo tanthauzo la: “Usiku ndi zimene wasonkhanitsa.”
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱلۡقَمَرِ إِذَا ٱتَّسَقَ
Ndi mwezi ukakwanira dangalira (lake),
Ərəbcə təfsirlər:
لَتَرۡكَبُنَّ طَبَقًا عَن طَبَقٖ
Ndithudi mudzachoka apa kunka apa (pa moyo uno mpakana umene uli nkudza).
Ərəbcə təfsirlər:
فَمَا لَهُمۡ لَا يُؤۡمِنُونَ
Kodi nchiyani chikuwaletsa iwo (okanira) kukhulupirira (Allah ndi kuuka kumanda, zisonyezo zake zitaonekera poyera)?
Ərəbcə təfsirlər:
وَإِذَا قُرِئَ عَلَيۡهِمُ ٱلۡقُرۡءَانُ لَا يَسۡجُدُونَۤ۩
Ndipo ikawerengedwa kwa iwo Qur’an, sagwetsa pansi nkhope zawo (modzichepetsa).
Ərəbcə təfsirlər:
بَلِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ يُكَذِّبُونَ
Koma amene sadakhulupirire akutsutsa basi (chifukwa cha makani ndi kudzikweza).
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِمَا يُوعُونَ
Ndipo Allah akudziwa (bwinobwino) zimene akuzisonkhanitsa.
Ərəbcə təfsirlər:
فَبَشِّرۡهُم بِعَذَابٍ أَلِيمٍ
Choncho, auze nkhani yachilango chopweteka.
Ərəbcə təfsirlər:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَهُمۡ أَجۡرٌ غَيۡرُ مَمۡنُونِۭ
Kupatula awo amene akhulupirira ndikuchita ntchito zabwino, kwa iwo kuli malipiro osatha.[410]
[410] Ayah iyi ikusonyeza kuti kukhulupilira kokha sikungampulumutse munthu ku chilango cha tsiku lachimaliziro, koma nkofunikanso kuchita ntchito zabwino; m’Qur’an paliponse pamene akutchula za chikhulupiliro akutchulanso za kuchita ntchito zabwino.
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: əl-İnşiqaq
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Tərcumənin mündəricatı

Qurani Kərimin şişyo dilinə mənaca tərcüməsi. Tərcüməçi:

Bağlamaq