Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Inshiqaaq   Versículo:

Sura Al-Inshiqaaq

إِذَا ٱلسَّمَآءُ ٱنشَقَّتۡ
Pamene thambo lidzang’ambike (kusonyeza mapeto ake),
Las Exégesis Árabes:
وَأَذِنَتۡ لِرَبِّهَا وَحُقَّتۡ
Ndikudzamvera lamulo la Mbuye wake; ndipo lidzayenera kutero,
Las Exégesis Árabes:
وَإِذَا ٱلۡأَرۡضُ مُدَّتۡ
Ndiponso pamene nthaka idzatambasulidwe (pogumuka mapiri ake ndikuchoka zitunda zake),
Las Exégesis Árabes:
وَأَلۡقَتۡ مَا فِيهَا وَتَخَلَّتۡ
Ndi kutaya zomwe zidali mkati mwake ndi kukhala yopanda kanthu,[405]
[405] Chimodzi mwa zinthu zoopsa zomwe zidzachitika tsiku lachimaliziro ndi kugwedezeka kwa nthaka mwamphamvu zedi mpaka idzalekana ndi mapiri amene ali zichiri zake zoletsa kugwedezeka kwake. Pachifukwa ichi idzatambasuka ndipo zomwe zidali mkati mwake zidzatulukira pamtunda; nthaka idzangokhala yopanda kanthu mkati mwake.
Las Exégesis Árabes:
وَأَذِنَتۡ لِرَبِّهَا وَحُقَّتۡ
Ndikudzamvera lamulo la Mbuye wake; ndipo lidzayenera kutero. (Choncho zikadzachitika zimenezi ndiye kuti munthu adzalandira mphoto ya zochita zake).[406]
[406] Allah pambuyo ponena zimenezi sadanene kuti chidzachitika chiyani. Alekera munthu mwini wake kuti aganizire chomwe chidzachitika zikadzapezeka zoopsa kuti aope kwambiri.
Las Exégesis Árabes:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡإِنسَٰنُ إِنَّكَ كَادِحٌ إِلَىٰ رَبِّكَ كَدۡحٗا فَمُلَٰقِيهِ
E iwe munthu! Ndithudi iwe ukubwerera kwa Mbuye wako (ndi zochita zako zabwino kapena zoipa), kubwerera kotsimikizika, ndipo iwe ukumana (ndi zotsatira za zochitachita zako).
Las Exégesis Árabes:
فَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِيَمِينِهِۦ
Tsono amene adzapatsidwe kaundula wa zochita zake kudzanja la manja,[407]
[407] Tsiku la chiweruziro munthu adzapatsidwa kaundula wake monga momwe zanenedwa mu Ayah 10 Surah Takwir, choncho ena adzapatsidwa ndi dzanja la kumanja; iwo ndiwo anthu abwino. Pomwe ena adzapatsidwa ndi dzanja la kumanzere, chakumbali yakumsana; iwowo ndiwo anthu oipa.
Las Exégesis Árabes:
فَسَوۡفَ يُحَاسَبُ حِسَابٗا يَسِيرٗا
Basi iye, adzawerengedwa, kuwerengedwa kopepuka,[408]
[408] Anthu ena adzawerengedwa popanda kufunsidwa mafunso pa zimene adachita, koma adzangowauza zabwino zawo ndi zoipa zawo ndipo pambuyo pake adzawakhululukira zoipazo ndi kudzawalipira pa zabwinozo. Iwowa ndiwo anthu abwino; chimenechi ndicho chiweruzo chofewa. Ena adzaweruzidwa pofunsidwa pa chilichonse m’zimene ankachita monga kuti “Bwanji ichi udachita? Bwanji ichi sudachite”? Iwowa ndiwo anthu oipa; chiwerengero chawo chidzakhala chokhwima.
Las Exégesis Árabes:
وَيَنقَلِبُ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ مَسۡرُورٗا
Ndipo adzabwerera kwa anthu ake (okhulupirira) ali wokondwa.
Las Exégesis Árabes:
وَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ وَرَآءَ ظَهۡرِهِۦ
Koma yemwe adzapatsidwe kaundula wa zochita zake chakumanzere kudzera kumbuyo kwa msana wake (chifukwa chomunyoza),
Las Exégesis Árabes:
فَسَوۡفَ يَدۡعُواْ ثُبُورٗا
Basi, iye adzaitana imfa (kuti imufikire; kuti afe apumule, koma siidzamufikira);
Las Exégesis Árabes:
وَيَصۡلَىٰ سَعِيرًا
Ndipo adzalowa ku Moto woyaka.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّهُۥ كَانَ فِيٓ أَهۡلِهِۦ مَسۡرُورًا
Kamba kakuti iye adali wokondwa; (kukondwa kwa machimo) pamodzi ndi anthu ake (osaganizira za mathero ake).
Las Exégesis Árabes:
إِنَّهُۥ ظَنَّ أَن لَّن يَحُورَ
Ndithudi, amaganiza kuti sadzabwerera (kwa Allah ndiponso sadzawerengedwa).
Las Exégesis Árabes:
بَلَىٰٓۚ إِنَّ رَبَّهُۥ كَانَ بِهِۦ بَصِيرٗا
Chifukwa ninji (asabwelere)? Ndithu Mbuye wake adali kumuona. (Choncho alipidwa zimene adachita).
Las Exégesis Árabes:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِٱلشَّفَقِ
Choncho ndikulumbilira kufiira kwa dzuwa (pamene likulowa).
Las Exégesis Árabes:
وَٱلَّيۡلِ وَمَا وَسَقَ
Ndi usiku ndi zimene wasonkhanitsa,[409]
[409] Kubalalikana masana ndi chizolowezi cha anthu ndi nyama chifukwa chofunafuna zinthu zothandiza pa moyo wawo. Tsono usiku ukabwera amasonkhana ndi kukhala pamodzi. Ndipo ili ndilo tanthauzo la: “Usiku ndi zimene wasonkhanitsa.”
Las Exégesis Árabes:
وَٱلۡقَمَرِ إِذَا ٱتَّسَقَ
Ndi mwezi ukakwanira dangalira (lake),
Las Exégesis Árabes:
لَتَرۡكَبُنَّ طَبَقًا عَن طَبَقٖ
Ndithudi mudzachoka apa kunka apa (pa moyo uno mpakana umene uli nkudza).
Las Exégesis Árabes:
فَمَا لَهُمۡ لَا يُؤۡمِنُونَ
Kodi nchiyani chikuwaletsa iwo (okanira) kukhulupirira (Allah ndi kuuka kumanda, zisonyezo zake zitaonekera poyera)?
Las Exégesis Árabes:
وَإِذَا قُرِئَ عَلَيۡهِمُ ٱلۡقُرۡءَانُ لَا يَسۡجُدُونَۤ۩
Ndipo ikawerengedwa kwa iwo Qur’an, sagwetsa pansi nkhope zawo (modzichepetsa).
Las Exégesis Árabes:
بَلِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ يُكَذِّبُونَ
Koma amene sadakhulupirire akutsutsa basi (chifukwa cha makani ndi kudzikweza).
Las Exégesis Árabes:
وَٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِمَا يُوعُونَ
Ndipo Allah akudziwa (bwinobwino) zimene akuzisonkhanitsa.
Las Exégesis Árabes:
فَبَشِّرۡهُم بِعَذَابٍ أَلِيمٍ
Choncho, auze nkhani yachilango chopweteka.
Las Exégesis Árabes:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَهُمۡ أَجۡرٌ غَيۡرُ مَمۡنُونِۭ
Kupatula awo amene akhulupirira ndikuchita ntchito zabwino, kwa iwo kuli malipiro osatha.[410]
[410] Ayah iyi ikusonyeza kuti kukhulupilira kokha sikungampulumutse munthu ku chilango cha tsiku lachimaliziro, koma nkofunikanso kuchita ntchito zabwino; m’Qur’an paliponse pamene akutchula za chikhulupiliro akutchulanso za kuchita ntchito zabwino.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Inshiqaaq
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar