কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ * - অনুবাদসমূহের সূচী


অর্থসমূহের অনুবাদ আয়াত: (1) সূরা: সূরা আল-বাইয়েনাহ

সূরা আল-বাইয়েনাহ

لَمۡ يَكُنِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ وَٱلۡمُشۡرِكِينَ مُنفَكِّينَ حَتَّىٰ تَأۡتِيَهُمُ ٱلۡبَيِّنَةُ
Amene adakanira (Allah ndi Mthenga Wake) mwa omwe adapatsidwa buku ndi opembedza mafano sadali olekana (ndi umbuli wawo ndi kusalabadira kwawo choona) mpaka pomwe chidawadzera chisonyezo choonekera poyera.[466]
[466] “Akafiri” omwe adapatsidwa buku, ndi Ayuda ndi Akhristu. “Amushirikina” ndi omwe adali kupembedza mafano. Tanthauzo la ma Ayah awa 1- 4 ndikuti asadatulukire Muhammad (s.a.w), Ayuda ndi Akhristu omwe adali ku Madina, pamene adali kuwauza opembedza mafano kuti: “Yayandikira nthawi yotulukira Mneneri. Ife tidzamtsatira, tidzakhala pamodzi ndi iye. Tidzakumenyani nkhondo mpaka kukugonjetsani.” Adali kuyembekezera kuti Mneneriyo adzakhala mwa iwo. Pamene adali kumva izi, opembedza mafano aja, adali odandaula. Iwonso adali kuyembekezera Mneneriyo; limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti: “Sadali olekana mpaka pomwe chidawadzera chisonyezo choonekera poyera.”
Apa ndiye kuti fuko lililonse mwa mafuko atatu aja lidali ndi mtima wopitiriza zipembedzo zawo, osaleka mpaka chiwafikire chisonyezo. Tanthauzo la “chisonyezo,” apa ndi Muhammad (s.a.w) monga Ayah yachiwiri yafotokozera.
Pamene adafika Mneneri, opembedza mafano aja ndiwo adayamba kumukhulupilira, koma Ayuda ndi Akhristu pamene adaona kuti Mneneri sali wochokera mwa iwo monga m’mene adali kuyembekezera adakhumudwa; ena mwa iwo adamkhulupilira pomwe ena sadamkhulupirire. Ili ndilo tanthauzo lakuti, “sadalekane omwe adapatsidwa mabuku mpaka pomwe chidawafikira chisonyezo.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
 
অর্থসমূহের অনুবাদ আয়াত: (1) সূরা: সূরা আল-বাইয়েনাহ
সূরাসমূহের সূচী পৃষ্ঠার নাম্বার
 
কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ - অনুবাদসমূহের সূচী

চেওয়া ভাষা আল-কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ-খালিদ ইবরাহীম বীতালা, সংস্করণ ২০২০ খ্রি.

বন্ধ