Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Ajet: (12) Sura: Sura Junus
وَإِذَا مَسَّ ٱلۡإِنسَٰنَ ٱلضُّرُّ دَعَانَا لِجَنۢبِهِۦٓ أَوۡ قَاعِدًا أَوۡ قَآئِمٗا فَلَمَّا كَشَفۡنَا عَنۡهُ ضُرَّهُۥ مَرَّ كَأَن لَّمۡ يَدۡعُنَآ إِلَىٰ ضُرّٖ مَّسَّهُۥۚ كَذَٰلِكَ زُيِّنَ لِلۡمُسۡرِفِينَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo vuto likamkhuza munthu amatipempha (m’kakhalidwe kake konse), chogona, chokhala kapena choimilira. Koma tikamchotsera vuto lomwe lidampeza, amayenda ngati sanatipempheko pa vuto Iomwe Iidamkhudza. Momwemo ndimo zakometseredwa kwa opyola malire zomwe ankachita.[217]
[217] Munthu vuto likamkhudza mthupi mwake, kapena pachuma chake ndi mwina motero apo mpomwe amazindikira za kufooka kwake. Amayamba kumkuwira Mbuye wake Allah ndi kumpempha m‘kakhalidwe kake konse- chogona, chokhala, choimilira kuti amchotsere mliri umene wamgwera. Koma Allah akamuyankha namchotsera vutolo amamfulatira Allah napitiriza kumlakwira naiwala ubwino wa Allah ngati kuti vuto silidamkhudze, ngati kutinso sadampempheko Allah. Ichi ndicho chikhalidwe cha anthu ambiri. Amadziwa Allah pomwe mavuto akawagwera. Koma akakhala pamtendere Allah amamuiwala.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Ajet: (12) Sura: Sura Junus
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje